Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

FUNSO 11

Kodi Chimachitika Nʼchiyani Munthu Akamwalira?

“Mpweya wake umachoka, ndipo iye amabwerera kunthaka. Pa tsiku limenelo zonse zimene amaganiza zimatheratu.”

Salimo 146:4

“Chifukwa amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa chilichonse . . . Chilichonse chimene dzanja lako lapeza kuti lichite, uchichite ndi mphamvu zako zonse, chifukwa ku Manda kumene ukupitako kulibe kugwira ntchito, kuganiza zochita, kudziwa zinthu kapena nzeru.”

Mlaliki 9:5, 10

“[Yesu] anauza ophunzira akewo kuti: ‘Mnzathu Lazaro ali mʼtulo, koma ndikupita kumeneko kukamudzutsa.’ Apa Yesu ankatanthauza kuti Lazaro wamwalira. Koma iwo ankaganiza kuti akunena za kugona tulo teniteni. Kenako Yesu anawauza mosapita mʼmbali kuti: ‘Lazaro wamwalira.’ ”

Yohane 11:11, 13, 14