Malo Amene Adzachititsa Kuti Mulemekezedwe
Pangani Dawunilodi:
1. Yehova, wolenga kumwamba,
M’mwamba simungakwanemo,
Ngakhalenso pano padziko.
Koma mwatipatsa mzimu.
Anthu anu akongoletsa
Malo olambirirawa.
Timadzipereka n’kumatumikira
Mosangalala.
(VESI LOKOMETSERA)
Zonsetu Yehova
Munatipatsa ndinu.
Zomwe tikupereka
Mwatipatsa ndinu.
(KOLASI)
Tikuthokozatu zonsezi,
Poimba mokweza mawu.
Ndi malo mwatipatsa
Tidikira madalitso.
2. Yehova munadziwa ndithu
Tinkafunika malowa,
Adzathandiza anthu anu
Kuyendabe m’njira zanu.
Pali ntchito yoti tigwire.
Malowa adzathandiza,
Pogwiratu ntchito ya Yesu
N’kuyendabe ndi gululi.
(VESI LOKOMETSERA)
Tim’patse zabwino
Nthawi ndi chuma chathu.
Ndinu woyenera ku—landira
Zonsezi.
(KOLASI)
Tikuthokozatu zonsezi,
Poimba mokweza mawu.
Ndi malo mwatipatsa
Tidikira madalitso.