Anzanga Apamtima
Pangani Dawunilodi:
1. Ndikuona aliyense
Ali ndi wocheza naye.
Ndikudziwa, ndiyenera
Anzangawa ndizisankha.
Ndizabwino kudziwatu
Komwe ndingapeze anthu
Ondikonda, abwinodi,
Omandilimbikitsadi.
(KOLASI)
Ndatsimikiza,
Inu Yehova.
Mundithandize
Kuti ndisankhe
Anzanga apamtima.
2. Mumtimamu ndikudziwa,
Ndikuchita zoyenera.
Mawu anu n’kawerenga,
Amandikhudzadi mtima.
Ndaonatu; ndadziwanso
Kopeza ‘nzanga abwino.
Tili ngati pachibale;
M‘lungu wandipatsa onse.
(KOLASI)
Ndatsimikiza,
Inu Yehova.
Mundithandize
Kuti ndisankhe
Anzanga apamtima.