Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nimayamikila Cilengedwe ca Mulungu

Nimayamikila Cilengedwe ca Mulungu

Daunilodi:

  1. 1. Maluŵa akumela pa phili

    Kucoka kumaphili mphepo ipita

    Dzuŵa nayo ikuŵala bwino,

    M’makumbi mbalame ziuluka.

    (MWANA WA KOLASI)

    Niyang’ana zinthu zabwino

    Nidzaonetsadi niyamikila.

    (KOLASI)

    Nimayamikila, cikondi ca M’lungu

    Ni cikulu, amanisamala

    Ni-kaona zinthu zimene Yehova ’manipatsa

    Anapanga Zonse m’cikondi.

    Nimayamikila.

    Niyamikila.

  2. 2. M’mwamba nionamonso mphamvu zake,

    Zonse anazipanga nikondwela nazo.

    Madzi nawonso yapita bwino m’nyanja

    Nyenyezinso ziwala na mwezi.

    (MWANA WA KOLASI)

    Niyang’ana zinthu zabwino

    Nidziŵa zocita, nidzayamikila.

    (KOLASI)

    Nimayamikila, cikondi ca M’lungu

    Ni cikulu, amanisamala.

    Ni-kaona zinthu zimene Yehova ’manipatsa

    Anapanga zonse m’cikondi

    Nimayamikila.

    (BILIJI)

    Niona nzelu na mphamvu

    Na ubwino wa M’lungu

    Ni wacikondi, niyamikila

    Nimayamikila

    (KOLASI)

    Nimayamikila, cikondi ca M’lungu

    Ni cikulu, amanisamala

    Ni-kaona zinthu zimene Yehova ’manipatsa

    Anapanga zonse m’cikondi

    Nimayamikila.

    Nimayamikila.

    Tiziyamikila.