Dziko Latsopano Lomwe Likubwera

Dziko Latsopano Lomwe Likubwera

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. M’maganizo taonani izi:

    Mukuona zinthu zochititsa chidwi

    Ana ‘kusewera

    M’dziko lomwe nkhawa zonse zatha.

    Anthu onse okhulupirika

    Akusamalira bwino dzikoli.

    Kulitu chitetezo​—

    Ndi mtendere mpaka kalekale.

    N’zosangalatsa,

    Yesu akulamulira

    M’dziko latsopano.

    (KOLASI)

    Chiyembekezo chathu

    Chili ngati nangula wathu,

    Chimawala ngatitu dzuwa

    Ngatitu tilidi

    M’dziko latsopano.

  2. 2. Taganizirani malo ake

    Mapiri, mitsinje, malo okongola.

    Uku ndiye kwanu.

    Mukutuluka m’nyumba mwanu,

    Pali wina wom’dziwa

    Wofunika kum’kumbatira

    Tikusangalala—

    Padutsa zaka osamuona

    Imfa yagonja

    N’chikondi chake

    M’dziko latsopano.

    (KOLASI)

    Chiyembekezo chathu

    Chili ngati nangula wathu,

    Chimawala ngatitu dzuwa

    Ngatitu tilidi

    M’dziko latsopano.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Mawu onse wanena

    Adzakwaniritsidwa ndithu.

    N’chifuniro cha Yehova

    Watipatsa zonse tinkafuna.

    (KOLASI)

    Chiyembekezo chathu

    Chili ngati nangula wathu,

    Chimawala ngatitu dzuwa

    Ngatitu tilidi

    M’dziko latsopano,

    M’dziko latsopano,

    M’dziko latsopano,

    M’dziko latsopano.