Chimwemwe Chosatha

Chimwemwe Chosatha

(Salimo 16:11)

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. M’mwamba mwadzaza nyenyezi

    Zikuwalatu.

    Masananso Kukongola

    M’matikondadi.

    M’nalenga nyanja ndi mtunda,

    Ndi zonse timaonazi

    Munamva bwino.

    (KOLASI)

    Tonse tikusangalala,

    N’za chipulumutso chathu,

    Ndi dziko latsopano.

    Kukondedwa ndi ’nu M’lungu

    Ndi mwayidi wapadera.

    Ndinutu m’matipatsa

    Chimwemwe chosatha.

  2. 2. Tili n’zonse zofunika

    Zosangalatsa

    Munatilenga mwaluso,

    Timamva bwino.

    Munatipatsatu mtima,

    Wofuna kukhala moyo

    Mpakatu kale.

    (KOLASI)

    Tonse tikusangalala,

    N’za chipulumutso chathu,

    Ndi dziko latsopano.

    Kukondedwa ndi ’nu M’lungu

    Ndi mwayidi wapadera.

    Ndinutu m’matipatsa

    Chimwemwe chosatha.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Popandatu Yesu

    Chimwemwe panalibe.

    Iyetu anatifera

    Ndiye chimwemwe n’chosatha.

    (KOLASI)

    Tonse tikusangalala,

    N’za chipulumutso chathu,

    Ndi dziko latsopano.

    Kukondedwa ndi ’nu M’lungu

    Ndi mwayidi wapadera.

    Ndinutu m’matipatsa

    Chimwemwe chosatha.

    (KOLASI)

    Tonse tikusangalala,

    N’za chipulumutso chathu,

    Ndi dziko latsopano.

    Kukondedwa ndi ’nu M’lungu

    Ndi mwayidi wapadera.

    Ndinutu m’matipatsa

    Chimwemwe chosatha.