Gwiritsani Ntchito Mphamvu Zanu Potumikira Yehova
Pangani Dawunilodi:
1. Ulitu mwana, zinkaphwekako
Kuchitatu zoyenera.
Unkakondanso kulalikira,
N’kupemphera nthawi zonse.
(KUKONZEKERA KOLASI)
Koma pomwe ukukula zinthu zingasinthe.
Ungakanike kugogoda m’makomo mu ‘tumiki.
Koma pomwe watalika chonde usasiye
Kutumikira Yehova,
Adzakudalitsa.
(KOLASI)
M’nyumba ya Yehova uli ndi malo,
Akuthandiza.
Ungamupatse Yehova zambiritu.
M’lungu amaona,
Amakukonda.
2. Pano wakula, zinthu zasinthadi,
Mayesero ayambanso.
Nkhawa nazo zachulukadi
Pemphera, M’lungu amamva.
(KUKONZEKERA KOLASI)
Pomwetu wakula uzichita zimene
Umaphunzira, udzasangalala ndithu.
Pomwe ukufuna kuti usankhe zochita,
Usaiwale Yehova,
Adzakudalitsa.
(KOLASI)
M’nyumba ya Yehova uli ndi malo,
Akuthandiza.
Ungamupatse Yehova zambiritu.
M’lungu amaona,
Amakukonda.
(VESI LOKOMETSERA)
M’tumikire ndi mphamvu zako.
N’zabwinodi, sungadzadandaule.
(KOLASI)
M’nyumba ya Yehova uli ndi malo,
Akuthandiza.
Ungamupatse Yehova zambiritu.
M’lungu amaona,
Amakukonda.
(VESI LOKOMETSERA)
M’tumikire ndi mphamvu zako.
N’zabwinodi, sungadzadandaule.
M’tumikire ndi mphamvu zako.
N’zabwinodi, sungadzadandaule.