“Timakobidi Tiwiri”
Pangani Dawunilodi:
1. Tochepa
N’tomwe ali nato.
Enatu
Akupereka zambiri zedi
Ndipo iye
Akudzimva wachabe.
Kodi M’lungu wake
Angalandire tochepa?
(KOLASI)
Kaya n’tochepa,
Tiperekebe
Ndipo M’lungu alandira.
Iye ndi wamkulu
Kuposa anthufe,
Kuposa mitima yathu.
Timpatse.
2. Kalekale
Zinkamuyenderadi.
Ankapereka
Zochulukanso, anali ndi mphamvu.
Pano zochepa
N’zomwe angakwanitse
Koma kwa Yehova
Zochepazo ndi zochuluka.
(KOLASI)
Kaya n’tochepa,
Tiperekebe
Ndipo M’lungu alandira.
Iye ndi wamkulu
Kuposa anthufe,
Kuposa mitima yathu.
Timpatse.
(VESI LOKOMETSERA)
Amamvetsatu tikapereka
Zochepa kapena zochuluka.
Sadzatiiwala.
(KOLASI)
Kaya n’tochepa,
Tiperekebe
Ndipo M’lungu alandira.
Iye ndi wamkulu
Kuposa anthufe,
Kuposa mitima yathu.
Tim’patse.
Tim’patse zomwe tingathe.