Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

NKHANI 67

Yehosafati Adalira Yehova

Yehosafati Adalira Yehova

KODI mukudziwa amuna’wa ndi zimene iwo akuchita? Iwo akumka ku nkhondo, ndipo amuna ali patsogolo’wo akuyimba. Koma mungafunse kuti: ‘Nchifukwa ninji oyimba’wo alibe malupanga ndi mikondo zomenyera nkhondo?’ Tiyeni tione.

Yehosafati ndiye mfumu ya ufumu wa mafuko awiri wa Israyeli. Iye akukhala ndi moyo pa nthawi imodzi-modzi ndi Mfumu Ahabu ndi Yezebeli ya ufumu wakumpoto wa mafuko 10. Koma Yehosafati ndi mfumu yabwino, ndipo atate wake Asa anali’nso mfumu yabwino kwambiri. Kwa zaka zambiri anthu a ufumu wakumwela wa mafuko awiri analinkukhala bwino.

Komano kanthu kena kakuchitika kochititsa anthu’wo mantha. Amithenga akusimbira Yehosafati kuti: ‘Gulu la nkhondo lalikulu lochokera ku maiko a Moabu, Amoni, ndi Phiri la Seiri akudza kudzakuukirani.’ Aisrayeli ambiri akusonkhana pa Yerusalemu kudzafuna chithandizo cha Yehova. Akumka ku kachisi, kumene’ko Yehosafati akupemphera kuti: ‘O Yehova Mulungu wathu, sitikudziwa chochita. Tathedwa nzeru ndi gulu la nkhondo lalikulu’li. Tikuyang’ana kwa inu kaamba ka chithandizo.’

Yehova akumvetsera, ndipo akutuma mmodzi wa atumiki ake kuuza anthu’wo kuti: ‘Nkhondo’yi si yanu, koma ya Mulungu. Simudzamenya. Ingopenyani, muone m’mene Yehova adzakupulumutsirani.’

Tsono m’mawa mwake Yehosafati akuwauza kuti: ‘Dalirani Yehova!’ Ndiyeno akuika oyimba patsogolo pa ankhondo’wo, ndipo pamene akuguba akuyimba zitamando kwa Yehova. Kodi mukudziwa chimene chikuchitika poyandikira ku nkhondo’ko? Yehova akuchitititsa ankhondo a adani’wo kumenyana okha-okha. Pofika iwo, wankondo ali yense wa adani’wo wafa!

Kodi sikunali kwanzeru kwa Yehosafati kudalira Yehova? Tidzakhala anzeru tikadalira Yehova.