Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

MUTU 17

‘Nzeru za Mulungu N’zozama’

‘Nzeru za Mulungu N’zozama’

1, 2. Kodi cholinga cha Yehova chokhudza tsiku la 7 chinali chiyani, nanga panachitika vuto liti?

 YEHOVA atalenga anthu kumapeto kwa tsiku la 6, anaona kuti “zonse zimene anapanga zinali zabwino kwambiri.” (Genesis 1:31) Koma kuchiyambi kwa tsiku la 7, Adamu ndi Hava anasankha kumvera Satana ndipo anagalukira Yehova. Anthu, omwe anali apadera kwambiri pa zinthu zonse zimene Yehova analenga padzikoli, anachimwa, sanalinso angwiro ndipo anali oti adzafa. Zimenezitu zinali zomvetsa chisoni kwambiri.

2 Zinaoneka ngati cholinga cha Yehova chokhudza tsiku la 7 chalephereka momvetsa chisoni. Tsikuli linali loti lidzatenga zaka masauzande ambiri ngati mmene zinalilinso ndi masiku ena 6 oyambirira aja. Yehova ananena kuti tsikuli likhale lopatulika ndipo linali loti likamadzatha, dziko lonse lapansi lidzakhala Paradaiso momwe muzidzakhala anthu angwiro. (Genesis 1:28; 2:3) Koma popeza kuti anthu sanamvere Mulungu, zomwe zinayambitsa mavuto aakulu, kodi zimenezi zikanatheka bwanji? Kodi Mulungu akanatani pamenepa? Zimene iye anachita zinasonyeza m’njira yapadera kwambiri kuti ndi wanzeru.

3, 4. (a) N’chifukwa chiyani tinganene kuti zimene Yehova anachita ulamuliro wake utaukiridwa mu Edeni ndi chitsanzo choti ali ndi nzeru zogometsa? (b) Kodi kudzichepetsa kuyenera kutichititsa kumakumbukira mfundo iti tikamaphunzira zokhudza nzeru za Yehova?

3 Yehova anachitapo kanthu nthawi yomweyo. Anapereka chilango kwa amene anasankha kuukira ulamuliro wakewo, ndipo pa nthawi imodzimodziyo, anasonyezanso kuti adzathetsa mavuto amene anali atangoyambika kumenewo. (Genesis 3:15) Njira imene Mulungu anasankha kuti agwiritse ntchito pothetsa mavutowo, inali yoti azidzachita zinthu pang’onopang’ono ndipo padzadutsa nthawi yaitali kwambiri mpaka pamene mavuto onse oyambitsidwa ndi oukira ulamuliro wake adzathetsedwe. Njirayi inali yosavuta koma yanzeru kwambiri moti tikhoza kuiphunzira komanso kuiganizira kwa moyo wathu wonse n’kumaonabe kuti ndi yosangalatsa. Ndiponso n’zosakayikitsa ngakhale pang’ono kuti njira imeneyi idzathandiza kuti cholinga cha Mulungu chikwaniritsidwe. Pogwiritsa ntchito njirayi Mulungu adzathetsa zoipa zonse, uchimo ndiponso imfa. Njirayi idzathandizanso kuti anthu okhulupirika akhale angwiro. Zonsezi zidzachitika tsiku la 7 lisanathe, moti ngakhale kuti ena anaukira ulamuliro wake, Yehova adzakhala kuti wakwaniritsa cholinga chake chokhudza dziko lapansi ndiponso anthu pa nthawi yake.

4 Kunena zoona, timagoma kwambiri tikaganizira nzeru zimenezi. M’pake kuti mtumwi Paulo analemba kuti ‘nzeru za Mulungu n’zozama.’ (Aroma 11:33) Tikamaphunzira njira zosiyanasiyana zimene Mulungu wasonyezera kuti ndi wanzeru, tiyenera kukhala odzichepetsa n’kumakumbukira kuti tikhoza kungodziwako kambali kakang’ono chabe ka nzeru zochuluka za Yehova. (Yobu 26:14) Choyamba tiyeni tikambirane zimene khalidwe logometsali limatanthauza.

Kodi Nzeru za Mulungu N’chiyani?

5, 6. Kodi pali kugwirizana kotani pakati pa kudziwa zinthu ndi kukhala wanzeru, nanga Yehova amadziwa zinthu zochuluka bwanji?

5 Kukhala wanzeru n’kosiyana ndi kudziwa zinthu. Makompyuta akhoza kusunga zinthu zambiri koma sitinganene kuti ndi anzeru. Komabe kudziwa zinthu n’kogwirizana ndi kukhala wanzeru. (Miyambo 10:14) Mwachitsanzo, ngati mukudwala matenda enaake aakulu, ndipo mukufuna malangizo amene angakuthandizeni kuti muchire, kodi mungafunse kwa munthu yemwe sadziwa kwenikweni zachipatala kapenanso sazidziwa n’komwe? Ayi. Choncho kudziwa zinthu molondola n’kofunika kwambiri kuti munthu akhaledi wanzeru.

6 Yehova amadziwa zinthu zochuluka kwambiri. Popeza ndi “Mfumu yamuyaya,” iye yekha ndi amene wakhalako kwa zaka zambirimbiri kuyambira kalekale. (Chivumbulutso 15:3) Ndipo amadziwa chilichonse chimene chakhala chikuchitika. Baibulo limati: “Palibe cholengedwa chimene Mulungu sangathe kuchiona. Chifukwa kwa iye zinthu zonse zili poonekera ndipo amatha kuziona bwinobwino moti ifeyo tidzayankha kwa Mulunguyo pa zochita zathu.” (Aheberi 4:13; Miyambo 15:3) Popeza ndi Mlengi, Yehova amadziwa bwino zimene analenga, ndipo wakhala akuona zochita zonse za anthu kuyambira pachiyambi. Amadziwanso zonse zimene zili mumtima mwa munthu. (1 Mbiri 28:9) Popeza anatipatsa ufulu wosankha, Yehova amasangalala akaona kuti tasankha zochita mwanzeru. Ndiponso iye ndi “Wakumva pemphero,” choncho anthu mamiliyoni ambirimbiri akamapemphera pa nthawi imodzi, iye amamva mapemphero onsewo. (Salimo 65:2) Ndipo n’zosachita kufunsa kuti Yehova amakumbukira chilichonse ndipo saiwala.

7, 8. Kodi Yehova amasonyeza bwanji kuti ndi womvetsa zinthu, wozindikira komanso wanzeru?

7 Sikuti Yehova amangodziwa zinthu. Amaonanso kugwirizana kwa zinthu komanso mmene mfundo zonse zikusonyezera chithunzi chonse cha nkhaniyo. Amapeza mfundo zofunika, kuziganizira, n’kugamulapo chifukwa choti amasiyanitsa chabwino ndi choipa komanso zofunika ndi zosafunika. Ndiponso sikuti iye amangoona zimene zikuoneka zokha koma amaonanso zomwe zili mumtima. (1 Samueli 16:7) Choncho Yehova amamvetsa ndiponso amazindikira mmene zinthu zilili ndipo zimenezi ndi zoposa kungodziwa zinthu. Koma kukhala ndi nzeru kumaposa zonsezi.

8 Munthu wanzeru ndi amene amadziwa mfundo zokhudza nkhani inayake, kuonetsetsa kuti wamvetsa mfundozo kenako n’kuzigwiritsa ntchito moyenera. N’chifukwa chake m’Baibulo mawu akuti “nzeru” amatanthauza “kugwira ntchito yomwe ikuyenda bwino.” Choncho Yehova amagwiritsa ntchito zimene akudziwa komanso luso lake lomvetsa zinthu kuti akwaniritse cholinga chake ndipo nthawi zonse zimamuyendera. Yehova amadziwa ndiponso kumvetsa chilichonse moti amasankha zochita mwanzeru kwambiri komanso amapeza njira yabwino yozikwaniritsira. Apatu amasonyeza kuti ndi wanzeru kwambiri. Yehova amasonyeza kuti zimene Yesu ananena ndi zoona. Iye anati: “Nzeru imatsimikizirika kuti ndi yolungama chifukwa cha ntchito zake.” (Mateyu 11:19) Zinthu zonse zimene Yehova analenga zimasonyeza kuti iye ndi wanzeru.

Chilengedwe Chimasonyeza Kuti Yehova Ndi Wanzeru

9, 10. (a) Kodi Yehova ali ndi nzeru zotani, nanga amazisonyeza bwanji? (b) Kodi selo limasonyeza bwanji kuti Yehova ndi wanzeru?

9 Kodi munachitapo chidwi ndi mmisiri amene amapanga zinthu zokongola zimene zimagwira ntchito bwino? Mmisiri woteroyo amasonyeza kuti ndi wanzeru kwambiri. (Ekisodo 31:1-3) Yehova ndi amene amapatsa munthu nzeru ndipo iye ndi wanzeru kuposa aliyense. Mfumu Davide inanena za Yehova kuti: “Ndimakutamandani chifukwa munandipanga modabwitsa ndipo zimenezi zimandichititsa mantha. Ntchito zanu ndi zodabwitsa, ine ndikudziwa bwino zimenezi.” (Salimo 139:14) Zoonadi, tikamaphunzira kwambiri zokhudza mmene thupi la munthu linapangidwira, m’pamenenso timagoma kwambiri ndi nzeru za Yehova.

10 Mwachitsanzo, moyo wanu unayamba pamene selo limodzi la dzira la amayi anu lomwe linakhwima linaphatikizana ndi umuna wa bambo anu. Pasanapite nthawi, selolo linayamba kugawikana. Inuyo, amene munakhalapo chifukwa cha kugawikana kumeneko, muli ndi maselo pafupifupi 100,000 biliyoni. Maselo amenewa ndi ang’onoang’ono kwambiri moti maselo pafupifupi 10,000 akhoza kukwanira pakanjere ka therere lobala. Komatu selo lililonse linapangidwa modabwitsa kwambiri. Selo lili ndi tinthu tambirimbiri m’kati mwake kuposa makina kapena fakitale ina iliyonse imene anthu apanga. Asayansi amati selo lili ngati mzinda umene uli ndi mpanda ndipo uli ndi mageti oyang’aniridwa bwino, olowera ndi otulukira. Mulinso misewu ndi magalimoto onyamula anthu, njira zolankhulirana, njira zopangira magetsi, malo otayira zinyalala ndi kukonzanso zinthu zogwiritsidwa kale ntchito, achitetezo komanso likulu la boma. Ndiponso m’maola ochepa chabe, selo likhoza kudzigawa pakati n’kukhala maselo awiri ofanana ndendende ndi loyamba lija.

11, 12. (a) Kodi n’chiyani chimachititsa kuti maselo a mwana amene ali m’mimba azikhala osiyanasiyana, ndipo zimenezi zikugwirizana bwanji ndi Salimo 139:16? (b) Kodi ubongo wa munthu umasonyeza bwanji kuti ‘tinapangidwa modabwitsa’?

11 Komabe sikuti maselo onse ndi ofanana. Maselo a mwana yemwe ali m’mimba mwa amayi ake akamapitiriza kugawikana, amayamba kugwira ntchito zosiyanasiyana. Ena amakhala maselo a mitsempha, ena a mafupa, a minofu, a magazi kapenanso a maso. Malangizo amene amathandiza kuti maselowa akhale osiyanasiyana chonchi amakhala mu DNA yomwe ili ngati laibulale ya selo. N’zochititsa chidwi kuti motsogoleredwa ndi mzimu, Davide anauza Yehova kuti: “Maso anu anandiona ngakhale pamene ndinali mluza. Ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku lanu.”​—Salimo 139:16.

12 Ziwalo zina zathupi la munthu n’zovuta kwambiri kuzimvetsa. Mwachitsanzo, taganizirani za ubongo. Asayansi ena amati ubongo ndi wovuta kwambiri kuumvetsa pa zinthu zonse zimene anazitulukira m’chilengedwe. Uli ndi maselo a mitsempha pafupifupi 100 biliyoni omwe ndi ochuluka mwina kufanana ndi nyenyezi zimene zili mu mlalang’amba wathuwu. Lililonse la maselo amenewa limapanga nthambi masauzande ambirimbiri zomwe zimalumikizana ndi maselo ena. Asayansi amanena kuti ubongo wa munthu ukhoza kusunga zinthu zonse zimene zili m’malaibulale onse apadzikoli, mwinanso kuposa pamenepo. Ngakhale kuti akhala akuphunzira zokhudza ubongo ‘wopangidwa modabwitsawu,’ asayansi amavomera kuti mwina sangamvetse zonse zokhudza mmene ubongowu umagwirira ntchito.

13, 14. (a) Kodi nyerere ndiponso zinthu zina za m’chilengedwe zimasonyeza bwanji kuti ndi “zanzeru mwachibadwa,” nanga zimenezi zimatiphunzitsa chiyani za Mlengi? (b) N’chifukwa chiyani tinganene kuti zinthu monga ulusi wa kangaude zinapangidwa “mwanzeru”?

13 Komabe, anthu ndi chitsanzo chimodzi chokha chosonyeza kuti Yehova analenga zinthu mwanzeru. Lemba la Salimo 104:24 limati: “Ntchito zanu ndi zochuluka, inu Yehova! Zonsezo munazipanga mwanzeru. Dziko lapansi ladzaza ndi zinthu zimene munapanga.” Zinthu zonse za m’chilengedwe zimasonyeza kuti Yehova ndi wanzeru. Mwachitsanzo, nyerere ndi “zanzeru mwachibadwa.” (Miyambo 30:24) Zimachita zinthu mwadongosolo m’magulu amene zimakhala. M’magulu ena, nyererezi zimasunga nsabwe za zomera n’kumapeza chakudya kuchokera ku nsabwezo ngati kuti ndi ziweto zake. Nyerere zina zimakhala ngati alimi ndipo zimalima tizomera tinatake tomwe sitichita maluwa komanso sitikhala ndi masamba. Zinthu zambiri zinalengedwa m’njira yoti zizichita zinthu modabwitsa kwambiri. Mwachitsanzo, ntchentche ikamauluka imagadabuzika ndipo ngakhale ndege yamakono kwambiri singathe kuchita zimenezo. Palinso mbalame zimene zimasamuka motsogoleredwa ndi nyenyezi, mphamvu ya maginito ya dziko kapenanso mapu amene zili nawo m’mutu. Asayansi ya zinthu zamoyo amatha zaka zambirimbiri akuphunzira zinthu zogometsa zimene nyamazi zimachita. N’zodziwikiratu kuti amene anapatsa nzeru zinthu zimenezi ndi wanzeru kwambiri.

14 Asayansi aphunzira zambiri kuchokera ku zinthu za m’chilengedwe ndipo zinthuzi zimasonyeza kuti Yehova ndi wanzeru. Moti pali asayansi ena omwe amapanga zinthu potengera zinthu za m’chilengedwe. Mwachitsanzo, mungachite chidwi ndi kukongola kwa ulusi wa kangaude. Koma munthu yemwe ndi injiniya angaone zoposa pamenepo. Amaona kuti ulusiwo ndi chinthu chokonzedwa mwaluso kwambiri. Ulusi wina wa kangaude womwe umaoneka ngati wosalimba ndi wolimba kwambiri kuposa chitsulo kapenanso ulusi wa zovala zimene zipolopolo sizingathe kuboola. Kodi ulusi wa kangaude ndi wolimba bwanji? Tiyerekeze kuti mwakulitsa ulusiwu mpaka kukhala waukulu ngati ukonde umene anthu amagwiritsa ntchito popha nsomba. Ulusi wa chonchi ukhoza kuimitsa ndege yomwe ikuuluka. Zoonadi, Yehova anapanga zinthu zonsezi “mwanzeru.”

Kodi ndani anakonza zoti zinthu zamoyo padzikoli zizikhala “zanzeru mwachibadwa”?

Zinthu Zakumwamba Zimasonyezanso Nzeru za Mulungu

15, 16. (a) Kodi nyenyezi zimasonyeza bwanji kuti Yehova ndi wanzeru? (b) Kodi zimene Yehova amachita popatsa angelo ntchito yokwanira zimasonyeza bwanji kuti ndi wanzeru?

15 Nzeru za Yehova zimaoneka m’zinthu zonse zimene anapanga. Nyenyezi zakumwamba, zimene tinakambirana kwambiri m’Mutu 5, zinaikidwa pamalo ake mwadongosolo. Chifukwa chakuti Yehova ndi wanzeru, anapanga “malamulo amene zinthu zakuthambo zimatsatira” moti nyenyezi zinaikidwa m’milalang’amba. (Yobu 38:33) Milalang’ambayo inaikidwa m’magulu ndipo magulu amenewo anaikidwanso m’magulu ena akuluakulu. M’pake kuti Yehova amanena kuti zinthu zakumwamba zimenezi ndi “gulu la nyenyezi.” (Yesaya 40:26) Komabe, pali gulu linanso limene limasonyeza bwino kuti Yehova ndi wanzeru.

16 Monga tinaonera m’Mutu 4, Mulungu ali ndi dzina la udindo lakuti “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba” chifukwa choti iye ndi Mtsogoleri Wamkulu wa gulu lalikulu kwambiri la angelo. Zimenezi zikusonyeza kuti iye ndi wamphamvu kwambiri. Koma ndi umboni wosonyezanso kuti ndi wanzeru. N’chifukwa chiyani tikutero? Taganizirani mfundo iyi: Nthawi zonse Yehova ndi Yesu amakhala akugwira ntchito. (Yohane 5:17) Choncho n’zomveka kuganiza kuti angelo, omwe ndi atumiki a Wam’mwambamwamba, nawonso amakhala otanganidwa nthawi zonse. Ndipo kumbukirani kuti angelo ndi anzeru komanso amphamvu kwambiri kuposa anthu. (Aheberi 1:7; 2:7) Komatu kwa zaka mabiliyoni, Yehova wakhala akupatsa angelo onse ntchito yokwanira yomwe amaigwira mosangalala. Iwo “amamvera mawu ake komanso kuchita zimene wanena.” (Salimo 103:20, 21) Zimenezitu zikusonyeza kuti Yehova ali ndi nzeru zochuluka kwambiri.

“Wanzeru Yekhayo”

17, 18. N’chifukwa chiyani Baibulo limatchula Yehova kuti “wanzeru yekhayo,” nanga n’chifukwa chiyani timagoma ndi nzeru zake?

17 Tikaganizira zonsezi, n’zosadabwitsa kuti Baibulo limasonyeza kuti Yehova ali ndi nzeru zopanda malire. Mwachitsanzo, limatchula Yehova kuti “wanzeru yekhayo.” (Aroma 16:27) Yehova yekha ndi amene ali ndi nzeru pa chilichonse. Nzeru zenizeni zimachokera kwa iye. (Miyambo 2:6) N’chifukwa chake Yesu, ngakhale kuti ndi wanzeru kwambiri pa zonse zimene Yehova analenga, sankadalira nzeru zake koma ankalankhula zimene Atate wake anamuuza.​—Yohane 12:48-50.

18 Mtumwi Paulo anafotokoza kuti nzeru za Yehova ndi zapadera kwambiri. Iye anati: “Ndithudi, madalitso amene Mulungu amapereka ndi ochuluka kwambiri. Nzeru zake n’zozama, ndiponso iye ndi wodziwa zinthu kwambiri. Ziweruzo zake ndi zovuta kuzimvetsa, ndipo ndani angatulukire njira zake?” (Aroma 11:33) Poyamba ndi mawu akuti “ndithudi,” Paulo anasonyeza kuti anakhudzidwa kwambiri komanso anagoma ndi nzeru za Yehova. Mawu a Chigiriki amene anagwiritsa ntchito palembali omwe anawamasulira kuti “kuzama,” ndi ofanana kwambiri ndi mawu akuti “phompho.” Choncho zimene Paulo ananena zimatithandiza kuona m’maganizo zimene ankatanthauza. Tikamaganizira nzeru za Yehova, zimakhala ngati tikuyang’ana m’chidzenje chozama kwambiri chomwe pansi pake sitingathe kuonapo, chachikulu kwambiri moti sitingathe kudziwa bwino kukula kwake, ndiponso chokanika kuchifotokoza ngakhalenso kuchijambula bwinobwino. (Salimo 92:5) Kudziwa zimenezi kuyeneratu kutichititsa kuti tikhale odzichepetsa.

19, 20. (a) N’chifukwa chiyani chiwombankhanga ndi chizindikiro choyenera cha nzeru za Mulungu? (b) Kodi Yehova wasonyeza bwanji kuti amatha kuoneratu zinthu za m’tsogolo?

19 Yehova ndi “wanzeru yekhayo” m’njira inanso: Ndi iye yekha amene angathe kudziwiratu za m’tsogolo. Kumbukirani kuti chiwombankhanga, chomwe chimaona patali, ndi chizindikiro cha nzeru za Yehova. Ziwombankhanga za mtundu winawake zimangolemera makilogalamu 5 okha, komatu maso ake amakhala akuluakulu kuposa a munthu wamkulu. Maso a chiwombankhanga ndi akuthwa kwambiri moti chili m’mwamba chimatha kuona kanthu kakang’ono kwambiri kamene kali pansi pamtunda wa mamita mahandiredi ochuluka, mwinanso makilomita kumene. Ponena za chiwombankhanga, Yehova anati: “Maso ake amaona kutali kwambiri.” (Yobu 39:29) Mofanana ndi zimenezi, Yehova akhoza ‘kuona kutali kwambiri,’ kapena kuti kudziwiratu zakutsogolo.

20 M’Baibulo muli maulosi ambirimbiri amene amasonyeza kuti Yehova akhoza kudziwiratu za m’tsogolo. Linaneneratu amene adzapambane pa nkhondo zina, kuyamba ndiponso kutha kwa maulamuliro amphamvu padziko lonse komanso njira zimene akukuluakulu asilikali adzagwiritse ntchito pa nkhondo. Nthawi zambiri Baibulo linkaneneratu zimenezi kudakali zaka mahandiredi angapo.​—Yesaya 44:25 mpaka 45:4; Danieli 8:2-8, 20-22.

21, 22. (a) N’chifukwa chiyani palibe chifukwa chomveka chonenera kuti Yehova amaoneratu zonse zimene mudzasankhe kuchita pa moyo wanu? Perekani chitsanzo. (b) Kodi timadziwa bwanji kuti Yehova sagwiritsa ntchito mphamvu zake mopanda chikondi?

21 Koma kodi zimenezi zikutanthauza kuti Mulungu anaoneratu kale zimene mudzasankhe pa moyo wanu? Anthu ena amene amakhulupirira kuti Mulungu anakonzeratu zonse zimene zidzachitike m’tsogolo angayankhe kuti inde. Koma maganizo amenewa amachititsa kuti Yehova azioneka ngati alibe nzeru chifukwa amasonyeza kuti sangalamulire luso lake lotha kudziwiratu zam’tsogolo. Mwachitsanzo, ngati mutakhala ndi luso loimba, kodi nthawi zonse mungamangoimba? Kuchita zimenezi kungasonyeze kuti simukuganiza bwino. Mofanana ndi zimenezi, Yehova ali ndi luso lotha kudziwiratu zam’tsogolo, koma sikuti amaligwiritsa ntchito nthawi zonse. Atamachita zimenezi, angakhale kuti sakulemekeza ufulu wosankha zochita umene anatipatsa. Komatu ufulu umenewu ndi mphatso yamtengo wapatali imene sadzatilanda.​—Deuteronomo 30:19, 20.

22 Anthu amene amakhulupirira kuti Yehova anakonzeratu zonse zimene zimachitika, amamuimba mlandu kuti ndi amene amachititsa zoipa zonse ndipo amaganiza kuti iye amagwiritsa ntchito mphamvu zake mopanda chikondi. Komatu limeneli ndi bodza lamkunkhuniza. Baibulo limaphunzitsa kuti Yehova “ali ndi mtima wanzeru.” (Yobu 9:4) Izi sizikutanthauza kuti ali ndi mtima weniweni. Koma nthawi zambiri Baibulo limagwiritsa ntchito mawu akuti mtima ponena za munthu weniweniyo kuphatikizapo zolinga zake komanso makhalidwe ake monga chikondi. Choncho mofanana ndi makhalidwe ake ena, nzeru za Yehova zimatsogoleredwa ndi chikondi.​—1 Yohane 4:8.

23. Kodi tiyenera kuchita chiyani popeza Yehova ndi wanzeru kwambiri kuposa ifeyo?

23 Nzeru za Yehova n’zodalirika kwambiri. Iye ndi wanzeru kwambiri kuposa ife. N’chifukwa chake Mawu ake amatilimbikitsa kuti: “Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, ndipo usamadalire luso lako lomvetsa zinthu. Uzimukumbukira m’njira zako zonse, ndipo iye adzawongola njira zako.” (Miyambo 3:5, 6) Tsopano tiyeni tiphunzire zambiri zokhudza nzeru za Yehova, kuti tikhale pa ubwenzi wolimba ndi Mulungu wanzeru zonse ameneyu.