Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

MUTU 19

‘Nzeru ya Mulungu Imaonekera mu Chinsinsi Chopatulika’

‘Nzeru ya Mulungu Imaonekera mu Chinsinsi Chopatulika’

1, 2. Kodi ndi “chinsinsi chopatulika” chiti chimene tiyenera kufunitsitsa kuchidziwa, ndipo n’chifukwa chiyani?

 ANTHUFE tikakhala kuti tikudziwa kapena kumvetsa zinthu zina zimene ena sakuzidziwa, nthawi zambiri zimativuta kusunga chinsinsi. Komabe Baibulo limati: “Kusunga chinsinsi ndi ulemerero wa Mulungu.” (Miyambo 25:2) Yehova, yemwe ndi Wolamulira Wamkulu ndiponso Mlengi, saulula zinthu zina kwa anthu mpaka nthawi yake itafika.

2 Komabe pali chinsinsi china chochititsa chidwi chimene Yehova anachiulula m’Mawu ake. Chimatchedwa kuti “chinsinsi chopatulika chokhudza chifuniro [cha Mulungu].” (Aefeso 1:9) Kudziwa chinsinsi chimenechi kungakuthandizeni kwambiri kuposa mmene zimakhalira tikangodziwa nkhani inayake yachinsinsi. Kungakuthandizeni kuti mudzapulumuke komanso kuti mumvetse bwino mfundo yoti Yehova ndi wanzeru kwambiri.

Ankachiulula Pang’onopang’ono

3, 4. N’chifukwa chiyani tinganene kuti ulosi wa pa Genesis 3:15 unali uthenga wachiyembekezo, ndipo unali ndi “chinsinsi chopatulika” chiti?

3 Cholinga cha Yehova chinali choti dziko lonse lapansi lidzakhale Paradaiso momwe muzidzakhala anthu angwiro. Komabe Adamu ndi Hava atachimwa, zinaoneka ngati cholingachi chalephereka. Koma nthawi yomweyo Mulungu anapeza njira yoti adzathetsere vutoli. Ananena kuti: “Ndidzaika chidani pakati pa iwe [njoka] ndi mkaziyo, komanso pakati pa mbadwa yako ndi mbadwa yake. Mbadwa ya mkaziyo idzaphwanya mutu wako, ndipo iwe udzaivulaza chidendene.”​—Genesis 3:15.

4 Amenewatu anali mawu ovuta kuwamvetsa. Kodi mkaziyu anali ndani? Kodi njokayo inali ndani? Nanga ndi ndani amene anali “mbadwa” imene idzaphwanye mutu wa njoka? Mayankho amene Adamu ndi Hava akanakhala nawo pa mafunsowa anali ongoganizira. Komabe, zimene Mulungu ananenazi unali uthenga wachiyembekezo kwa ana okhulupirika a anthu awiri osakhulupirikawa. Ana awowo akanakhala otsimikizira kuti Yehova adzathetsa zoipa zonse, uchimo ndipo zofuna zake zidzachitika. Koma kodi zimenezi zinali zoti zidzachitika bwanji? Pamenepa m’pamene panagona chinsinsi. Baibulo limati chinsinsi chimenechi ndi “nzeru ya Mulungu yomwe ndi nzeru yobisika, imene inaonekera mu chinsinsi chopatulika.”​—1 Akorinto 2:7.

5. Perekani chitsanzo chosonyeza chifukwa chake Yehova anaulula chinsinsi chake pang’onopang’ono.

5 Popeza Yehova ndi “Woulula zinsinsi,” anakonza zoti pakapita nthawi adzaulule mfundo zofunikira zokhudza chinsinsi chimenechi. (Danieli 2:28) Koma anakonza zoti azidzachita zimenezi pang’onopang’ono. Mwachitsanzo, taganizirani zimene bambo wachikondi angayankhe mwana wake wamng’ono atamufunsa kuti, “Kodi adadi, ineyo ndinachokera kuti?” Bambo wanzeru amauza mwanayo zinthu zokhazo zimene angazimvetse. Koma mwanayo akamakula, bambo akewo amayamba kumuuza zambiri. Mofanana ndi zimenezi, Yehova amadziwa nthawi yabwino yoti aululire anthu ake mfundo zokhudza zimene iye akufuna kuchita.​—Miyambo 4:18; Danieli 12:4.

6. (a) Kodi cholinga cha pangano n’chiyani? (b) N’chifukwa chiyani Yehova anachita mapangano ndi anthu?

6 Ndiye kodi Yehova ankaulula bwanji zimenezi? Ankaziulula pochita mapangano osiyanasiyana ndi anthu. N’kutheka kuti nthawi ina munasainiranapo pangano ndi munthu wina, kaya linali lokhudza kugula nyumba kapena kubwerekana ndalama. Pangano loterolo limatsimikizira mwalamulo kuti aliyense adzachita zimene mwagwirizana. Popeza mawu a Yehova ndi okwanira kutsimikizira kuti adzakwaniritsa zimene walonjeza, n’chifukwa chiyani ankafunika kuchita mapangano ndi anthu? N’zoonadi kuti nthawi zonse amakwaniritsa mawu ake, komabe mokoma mtima nthawi zina Yehova amachita pangano ndi anthu pofuna kutsimikizira kuti zimene wanena zidzachitikadi. Mapangano odalirikawa, amathandiza anthu omwe si angwirofe kuti tisamakayikire ngakhale pang’ono kuti iye adzakwaniritsa zimene walonjeza.​—Aheberi 6:16-18.

Anachita Pangano ndi Abulahamu

7, 8. (a) Kodi Yehova anapanga pangano lotani ndi Abulahamu, ndipo zinathandiza anthu kudziwa chiyani zokhudza chinsinsi chopatulika? (b) Kodi Yehova anafotokoza zinthu ziti pang’onopang’ono poulula banja limene mbadwa yolonjezedwa idzachokere?

7 Patatha zaka zoposa 2,000 kuchokera pamene anthu anathamangitsidwa m’Paradaiso, Yehova anauza mtumiki wake wokhulupirika Abulahamu kuti: “Ndidzachulukitsadi mbadwa zako ngati nyenyezi zakumwamba . . . Kudzera mwa mbadwa yako, mitundu yonse yapadziko lapansi idzapeza madalitso chifukwa chakuti wamvera mawu anga.” (Genesis 22:17, 18) Limeneli silinali lonjezo chabe. Pofuna kutsimikizira kuti adzakwaniritsadi zimenezi, pamenepa Yehova anapanga pangano ndi Abulahamu ndipo kenako analumbira. (Genesis 17:1, 2; Aheberi 6:13-15) N’zochititsa chidwi kuti Ambuye Wamkulu Koposa analonjeza mwalamulo kuti adzadalitsa anthu.

‘Ndidzachulukitsa mbadwa zako ngati nyenyezi zakumwamba’

8 Pangano la Abulahamu linaulula zoti wolonjezedwayo adzakhala munthu, chifukwa Yehova anati adzakhala mbadwa ya Abulahamu. Koma kodi munthu wake ndi ndani? Patapita nthawi, Yehova anaulula kuti pa ana a Abulahamu, mbadwayo idzachokera mwa Isaki. Pa ana awiri a Isaki, Yakobo ndi amene anasankhidwa. (Genesis 21:12; 28:13, 14) Kenako, Yakobo ananena mawu awa okhudza mmodzi wa ana ake aamuna 12: “Ndodo yachifumu sidzachoka kwa Yuda, ndiponso chibonga cha wolamulira sichidzachoka pakati pa mapazi ake, mpaka Silo [kapena kuti, “Mwini Wake,” mawu a m’munsi] atabwera. Ndipo mitundu ya anthu idzamumvera.” (Genesis 49:10) Tsopano zinadziwika kuti mbadwayo idzakhala mfumu ndipo idzachokera kwa Yuda.

Anachita Pangano ndi Aisiraeli

9, 10. (a) Kodi Yehova anachita pangano liti ndi Aisiraeli, nanga panganolo linkawateteza bwanji? (b) Kodi Chilamulo chinasonyeza bwanji kuti anthu ankafunikira dipo?

9 M’chaka cha 1513 B.C.E., Yehova anachitanso zinthu zina zimene zinathandiza kuti mbali zina zokhudza chinsinsi chopatulika zidziwike. Anachita pangano ndi Aisiraeli omwe anali mbadwa za Abulahamu ndipo limeneli linali pangano la Chilamulo cha Mose. Ngakhale kuti panganoli silikugwiranso ntchito panopa, linali lofunika kwambiri kuti cholinga cha Yehova chobweretsa mbadwa yolonjezedwa chikwaniritsidwe. N’chifukwa chiyani tikutero? Taganizirani zinthu zitatu izi. Choyamba, Chilamulo chinali ngati khoma loteteza. (Aefeso 2:14) Malamulo olungama a m’Chilamulochi ankasiyanitsa Ayuda ndi anthu a mitundu ina. Choncho Chilamulo chinateteza mzere wobadwira wa mbadwa yolonjezedwa. Zimenezi zinathandiza kuti mtundu wa Aisiraeli ukhalepobe mpaka nthawi imene Mulungu anatumiza Mesiya kuti adzabadwire mu fuko la Yuda.

10 Chachiwiri, Chilamulo chinasonyeza bwino kuti anthu ankafunikira dipo. Popeza Chilamulo chinali changwiro, chinathandiza Aisiraeli kudziwa kuti anthu ochimwa sangathe kuchitsatira popanda kulakwitsa chilichonse. Choncho chinathandiza “kuti machimo aonekere, mpaka mbadwa imene inapatsidwa lonjezolo itafika.” (Agalatiya 3:19) Nsembe za nyama zimene Aisiraeli anauzidwa kuti azipereka sizinkaphimbiratu machimo a anthu. Mogwirizana ndi zimene Paulo ananena, “n’zosatheka kuti magazi a ng’ombe zamphongo ndi mbuzi achotseretu machimo.” Choncho nsembe zimenezi zinkangoimira nsembe ya dipo ya Khristu. (Aheberi 10:1-4) Kwa Ayuda okhulupirika, pangano la Chilamulo linali ‘wowayang’anira amene anawatsogolera kwa Khristu.’​—Agalatiya 3:24.

11. Kodi pangano la Chilamulo linathandiza mtundu wa Isiraeli kukhala ndi chiyembekezo chabwino chiti, koma n’chifukwa chiyani Aisiraeli ambiri sanakhale ndi chiyembekezo chimenechi?

11 Chachitatu, pangano limeneli linathandiza Aisiraeli kuti akhale ndi chiyembekezo. Yehova anawauza kuti akadzakhala okhulupirika pa zimene anapangana naye, adzakhala ‘ufumu wa ansembe komanso mtundu woyera.’ (Ekisodo 19:5, 6) Patapita nthawi anthu oyambirira oti akakhale mafumu ndi ansembe kumwamba, anachokeradi mu mtundu wa Isiraeli. Komabe Aisiraeli ambiri sanatsatire pangano la Chilamulo ndipo anakana mbadwa yomwe inali Mesiya, choncho anataya mwayiwu. Ndiyeno kodi Yehova akanasankha ndani kuti alowe m’malo mwawo? Nanga pakanakhala kugwirizana kotani pakati pa anthu osankhidwawo ndi mbadwa yolonjezedwa? Mulungu anaulula mbali za chinsinsi chopatulika zimenezi pa nthawi yake.

Anachita Pangano la Ufumu ndi Davide

12. Kodi Yehova anachita pangano lotani ndi Davide, nanga linathandiza anthu kudziwa mfundo zina ziti zokhudza chinsinsi chopatulika cha Mulungu?

12 M’zaka za m’ma 1,000 B.C.E., Yehova anaululanso zinthu zina zokhudza chinsinsi chopatulika pamene anachita pangano linanso. Analonjeza Davide, yemwe anali mfumu yokhulupirika kuti: ‘Ndidzachititsa kuti mbadwa yako, ikhale mfumu ndipo ndidzachititsa kuti ufumu wake ukhazikike. Ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu mpaka kalekale.’ (2 Samueli 7:12, 13; Salimo 89:3) Tsopano zinadziwika kuti mbadwa yolonjezedwa idzabadwira m’banja la Davide. Koma kodi munthu wamba angalamulire mpaka kalekale? (Salimo 89:20, 29, 34-36) Nanga kodi angathe kupulumutsa anthu ku uchimo ndi imfa?

13, 14. (a) Mogwirizana ndi Salimo 110, kodi Yehova anailonjeza chiyani Mfumu yake yodzozedwa? (b) Kodi ndi mfundo zina ziti zokhudza mbadwa yolonjezedwa zimene zinadziwika kudzera mwa aneneri a Yehova?

13 Davide anauziridwa kulemba kuti: “Yehova anauza Ambuye wanga kuti: ‘Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.’ Yehova walumbira ndipo sadzasintha maganizo. Iye wati: ‘Iwe ndiwe wansembe mpaka kalekale, mofanana ndi unsembe wa Melekizedeki!’” (Salimo 110:1, 4) Mawu a Davidewa ankanena za mbadwa yolonjezedwa, kapena kuti Mesiya. (Machitidwe 2:35, 36) Mfumu imeneyi inali yoti izidzalamulira ili kumwamba “kudzanja lamanja” la Yehova, osati ili ku Yerusalemu. Zimenezi zinasonyeza kuti Mfumuyi sidzalamulira ku Isiraeli kokha koma padziko lonse lapansi. (Salimo 2:6-8) Apa mfundo zinanso zinadziwika. Onani kuti Yehova analumbira kuti Mesiya adzakhala “wansembe . . . mofanana ndi unsembe wa Melekizedeki.” Mofanana ndi Melekizedeki, yemwe anali mfumu ndiponso wansembe m’nthawi ya Abulahamu, mbadwa imene inkabwerayo inali yoti idzasankhidwa mwachindunji ndi Mulungu kuti ikhale Mfumu ndiponso Wansembe.​—Genesis 14:17-20.

14 M’zaka zotsatira, Yehova anagwiritsa ntchito aneneri ake poulula mfundo zina zokhudza chinsinsi chake chopatulika. Mwachitsanzo, Yesaya anaulula kuti mbadwayo idzapereka moyo wake ngati nsembe. (Yesaya 53:3-12) Mika ananeneratu kumene Mesiya adzabadwire. (Mika 5:2) Ndipo Danieli analosera za nthawi yeniyeni imene Mesiya adzayambe utumiki wake komanso nthawi imene adzafe.​—Danieli 9:24-27.

Chinsinsi Chopatulika Chinadziwika

15, 16. (a) Kodi zinachitika bwanji kuti Mwana wa Yehova ‘abadwe kudzera mwa mkazi’? (b) N’chifukwa chiyani Yesu anali woyenera kulowa ufumu wa Davide, nanga ndi liti pamene anakhala mbadwa yolonjezedwa?

15 Sizinkadziwika kuti maulosiwa adzakwaniritsidwa bwanji mpaka pamene mbadwayo inabwera. Lemba la Agalatiya 4:4 limati: “Nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake, amene anabadwa kudzera mwa mkazi.” M’chaka cha 2 B.C.E., mngelo anauza namwali wina wa Chiyuda dzina lake Mariya, kuti: “Mvetsera! Udzakhala woyembekezera n’kubereka mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina lakuti Yesu. Ameneyu adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wam’mwambamwamba. Yehova Mulungu adzamupatsa mpando wachifumu wa Davide atate wake. . . . “Mzimu woyera udzafika pa iwe ndipo mphamvu ya Wam’mwambamwamba idzakuphimba. Pa chifukwa chimenechi amene adzabadweyo adzatchedwa woyera, Mwana wa Mulungu.”​—Luka 1:31, 32, 35.

16 Kenako, Yehova anasamutsa moyo wa Mwana wake kuchoka kumwamba n’kuuika m’mimba mwa Mariya moti Mwanayo anabadwa kudzera mwa mkazi. Mariya sanali wangwiro. Koma Yesu sanatengere kupanda ungwiro kwa Mariya, chifukwa Yesuyo anali “Mwana wa Mulungu.” Komabe popeza makolo ake anali mbadwa za Davide, Yesu anali woyenera mwachibadwa ndiponso mwalamulo kulowa ufumu wa Davide. (Machitidwe 13:22, 23) Pamene Yesu ankabatizidwa m’chaka cha 29 C.E., Yehova anamudzoza ndi mzimu woyera, n’kunena kuti: “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa.” (Mateyu 3:16, 17) Apa tsopano mbadwa ija inafika. (Agalatiya 3:16) Imeneyi inali nthawi yoti Mulungu aulule zinthu zinanso zokhudza chinsinsi chopatulika.​—2 Timoteyo 1:10.

17. Kodi ndi mfundo ziti zokhudza lemba la Genesis 3:15 zimene zinadziwika?

17 Pamene Yesu ankachita utumiki wake, anathandiza anthu kudziwa kuti njoka yotchulidwa pa Genesis 3:15 ndi Satana ndipo mbewu ya njokayo ndi otsatira a Satana. (Mateyu 23:33; Yohane 8:44) Patapita nthawi, zinadziwika mmene onsewa adzawonongedwere moti sadzapezekanso. (Chivumbulutso 20:1-3, 10, 15) Kenako zinadziwikanso kuti mkazi ndi “Yerusalemu wam’mwamba,” kapena kuti mkazi wa Mulungu. Imeneyi ndi mbali yakumwamba ya gulu la Yehova lopangidwa ndi angelo okhulupirika. a​—Agalatiya 4:26; Chivumbulutso 12:1-6.

Pangano Latsopano

18. Kodi cholinga cha “pangano latsopano” n’chiyani?

18 Pa mfundo zonse zokhudza chinsinsi chopatulika zimene zinadziwika, mwina mfundo yapadera kwambiri inali imene Yesu anauza ophunzira ake usiku wake womaliza pamene ananena zokhudza “pangano latsopano.” (Luka 22:20) Mofanana ndi pangano la Chilamulo cha Mose, pangano latsopanoli linali loti lidzachititsa kuti pakhale ‘ufumu wa ansembe.’ (Ekisodo 19:6; 1 Petulo 2:9) Komabe anthu a m’pangano limeneli sanali Aisiraeli enieni koma “Isiraeli wa Mulungu,” yemwe ndi otsatira a Khristu okhulupirika omwenso ndi odzozedwa. (Agalatiya 6:16) Anthu a m’pangano latsopano amenewa limodzi ndi Yesu adzathandiza anthu okhulupirika kuti alandire madalitso.

19. (a) Kodi n’chifukwa chiyani pangano latsopano linathandiza kuti pakhale ‘ufumu wa ansembe’? (b) N’chifukwa chiyani Akhristu odzozedwa amatchedwa kuti “cholengedwa chatsopano,” ndipo ndi angati adzalamulire limodzi ndi Khristu kumwamba?

19 Koma kodi n’chifukwa chiyani pangano latsopano limathandiza kuti pakhale ‘ufumu wa ansembe’ umene udzadalitse anthu? N’chifukwa chakuti m’malo motsutsa ophunzira a Khristu kuti ndi ochimwa, panganoli limachititsa kuti machimo awo akhululukidwe pogwiritsa ntchito nsembe ya Khristuyo. (Yeremiya 31:31-34) Zikatero Yehova amawaona kuti ndi olungama, kapena kuti opanda uchimo, ndipo amawatenga kuti akhale ana ake n’kuwadzoza ndi mzimu woyera. (Aroma 8:15-17; 2 Akorinto 1:21) Choncho ‘amabadwanso mwatsopano n’kukhala ndi chiyembekezo chodalirika chimene anawasungira kumwamba.’ (1 Petulo 1:3, 4) Popeza anthu analengedwa kuti azikhala padzikoli osati kupita kumwamba, Akhristu odzozedwa ndi mzimu omwe adzapite kumwamba amatchedwa “cholengedwa chatsopano.” (2 Akorinto 5:17) Baibulo limanena kuti anthuwa, omwe ndi okwana 144,000, azidzalamulira anthu okhala padzikoli.​—Chivumbulutso 5:9, 10; 14:1-4.

20. (a) Kodi ndi mfundo iti yokhudza chinsinsi chopatulika imene inadziwika mu 36 C.E.? (b) Kodi ndi ndani adzasangalale ndi madalitso amene Abulahamu analonjezedwa?

20 Akhristu odzozedwa amenewa limodzi ndi Yesu amakhala ‘mbadwa ya Abulahamu.’ b (Agalatiya 3:29) Oyamba amene anasankhidwa anali Ayuda. Koma m’chaka cha 36 C.E., mfundo inanso yokhudza chinsinsi chopatulika inadziwika: Anthu omwe si Ayuda nawonso adzakhala m’gulu la anthu okalamulira ndi Yesu. (Aroma 9:6-8; 11:25, 26; Aefeso 3:5, 6) Koma kodi Akhristu odzozedwa okha ndi amene adzasangalale ndi madalitso amene Abulahamu analonjezedwa? Ayi. Nsembe ya Yesu imathandiza dziko lonse. (1 Yohane 2:2) Patapita nthawi, Yehova anathandiza anthu kudziwa kuti “khamu lalikulu” la anthu omwe chiwerengero chawo n’chosadziwika, adzapulumuka dziko la Satana likamadzawonongedwa. (Chivumbulutso 7:9, 14) Anthu enanso ambirimbiri adzaukitsidwa ndipo akhoza kudzakhala ndi moyo mpaka kalekale m’Paradaiso.​—Luka 23:43; Yohane 5:28, 29; Chivumbulutso 20:11-15; 21:3, 4.

Nzeru za Mulungu Ndiponso Chinsinsi Chopatulika

21, 22. Kodi chinsinsi chopatulika cha Yehova chimasonyeza bwanji nzeru zake?

21 Chinsinsi chopatulika chinasonyeza “mbali zosiyanasiyana za nzeru za Mulungu” m’njira yodabwitsa kwambiri. (Aefeso 3:8-10) Yehova anasonyeza kuti alidi ndi nzeru zozama pokonza chinsinsichi n’kumachiulula pang’onopang’ono. Anadziwa kuti anthu sangathe kumvetsa zinthu zozamazi kamodzin’kamodzi. Ndipo chifukwa choti ankachiulula pang’onopan’gono, anapatsa anthu mwayi woti asonyeze kuti amamudalira kapena ayi.​—Salimo 103:14.

22 Yehova anasonyezanso kuti ndi wanzeru kuposa aliyense pamene anasankha Yesu kuti akhale Mfumu. Mwana wa Yehova ameneyu ndi wodalirika kwambiri kuposa munthu kapena mngelo aliyense. Pamene anali munthu padzikoli, Yesu anakumana ndi mavuto osiyanasiyana choncho amamvetsa bwino mavuto a anthu. (Aheberi 5:7-9) Nanga bwanji anthu amene adzalamulire naye limodzi? Kwa zaka zambirimbiri, Yehova wakhala akudzoza amuna ndi akazi osiyanasiyana ochokera m’mitundu yonse ndiponso zilankhulo zonse. Palibe vuto limene tingakumane nalo lomwe aliyense wa anthu amenewa sanakumanepo nalo n’kuthana nalo. (Aefeso 4:22-24) Zidzakhalatu zosangalatsa kwambiri kulamuliridwa ndi mafumu ndi ansembe achifundo amenewa.

23. N’chifukwa chiyani ndi mwayi waukulu kudziwa chinsinsi chopatulika, ndipo tiyenera kuchita chiyani?

23 Mtumwi Paulo analemba kuti: “Chinsinsi chopatulika chimene dziko silinachidziwe ndiponso chinali chobisika kwa mibadwo yakale . . . chaululidwa kwa oyera ake.” (Akolose 1:26) Zoonadi, Akhristu odzozedwa, omwe ndi oyera a Yehova, amvetsa zinthu zambiri zokhudza chinsinsi chopatulika, ndipo amauzanso anthu mamiliyoni ambiri. Tonsefe tili ndi mwayi waukulu kwambiri. Yehova ‘watiululira chinsinsi chake chopatulika chokhudza chifuniro chake.’ (Aefeso 1:9) Tiyeni tiziuza ena chinsinsi chosangalatsachi kuti nawonso athe kuona nzeru zosaneneka za Yehova Mulungu.

a “Chinsinsi chopatulika chokhudza kukhala odzipereka kwa Mulungu,” chinadziwikanso kudzera mwa Yesu. (1 Timoteyo 3:16) Kwanthawi yaitali sizinkadziwika ngati munthu angakhalebe wokhulupirika kwa Yehova pa chilichonse. Koma Yesu anasonyeza kuti zimenezi n’zotheka. Anakhalabe wokhulupirika ngakhale kuti Satana anamuyesa m’njira zosiyanasiyana.​—Mateyu 4:1-11; 27:26-50.

b Yesu anachitanso “pangano la ufumu” ndi gulu lomweli. (Luka 22:29, 30) Apatu Yesu anapangana ndi anthu a mu “kagulu ka nkhosa” kameneka kuti adzalamulire naye limodzi kumwamba monga mbali yachiwiri ya mbadwa ya Abulahamu.​—Luka 12:32.