Nyimbo 98
Fesani Mbewu za Ufumu
1. Akapolonu a Yehova
Amene mwadzipereka,
Bwerani kuntchito ya ’Mbuye
Ndipo muzimutsanzira.
Muzifesa mbewu za cho’nadi
M’mitima ya omvetsera.
Mukakhulupirika kwa Mulungu
Inde mudzamulemekeza.
2. Mbewu zina zomwe mufesa
Zidzagweratu pamwala.
Zidzakuladi kwa kanthawi
Pambuyo pake n’kufota.
Minga ikatsamwitsa cho’nadi
Amatengeka ndi dziko.
Zina zidzapeza nthaka yachonde
Ndiponso zidzakula bwino.
3. Kuti ntchito iyende bwino
Khama lanu n’lofunika.
Mukaleza mtima ndi anthu
Angakhozedi kusintha.
Mwa kukhala atcheru mungathe
Kuwathetseradi mantha.
Mungakolole zipatso makumi
Atatu kapena kuposa
(Onaninso Mat. 13:19-23; 22:37.)