Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 8

Mgonero wa Ambuye

Mgonero wa Ambuye

(Mateyo 26:26-30)

1. Atate wathu wakumwamba,

Usikuwu n’ngwapadera!

Pa Nisani fotini panaoneka

Chikondi, nzeru ndi mphamvu.

Mwanawankhosa anadyedwa,

Is’raeli namasuka.

Kenako Mbuye anakhetsa magazi

Kukwaniritsa ulosiwo.

2. Tasonkhana pamaso panu.

Tadza ngati nkhosa zanu

Kukutamandani pa chikondi chanu,

Dzina lanu tilikweze.

Tisunge Chikumbutso ichi,

m’mitima ndi m’maganizo.

Tidzamutsatira Khristu nthawi zonse

Kuti tidzaupeze moyo.

(Onanino Luka 22:14-20; 1 Akor. 11:23-26.)