Nyimbo 77
Muzikhululuka
(Salimo 86:5)
1. Mwachikondi M’lungu
Mwa Yesu anakonza
Kuti tikhululukidwe
Ndi kuthetsadi imfa.
Ngati tilidi olapa,
Ndipo titamupempha,
Pogwiritsa ntchito
Dipo Atikhululukira.
2. Ngati titsanzira
Mulungu wakumwamba
Kukhululukira ena
Tidzakhululukidwa.
Tikhale ololerana,
Tisakhale odana
Koma olemekezana
Komanso okondana.
3. Tikhale n’chifundo,
Chidzatithandizadi
Kusasunga chakukhosi
Kapenanso chidani.
Tikatsanzira Yehova
Maka chikondi chake
Tidzakhululukirana
Tidzafanana naye.
(Onaninso Mat. 6:12; Aef. 4:32; Akol. 3:13.)