Nyimbo 7
Tidzipereke Monga Akhristu
(Aheberi 10:7, 9)
1. Yehova analengatu
Chilengedwe chonse,
Dzikoli ndi mlengalenga
Zonsezi ndi zake.
M’lungu watipatsa moyo
Wasonyeza kuti
Ndi woyenera kum’tamanda
Ndiponso kum’lambira.
2. Yesu anabatizidwa
Nanena m’pemphero:
‘Ndabwera kuti ndichite
Chifuniro chanu.’
Anatuluka m’Yo’dano
Monga wodzozedwa,
Kuti atumikire M’lungu
Monga wodzipereka.
3. Yehova, ife tabwera
Kukutamandani.
Tadzipereka kwa inu
Ndipo tadzikana.
Munapereka Mwana’nu,
Nalipira dipo.
Tasiyatu zofuna zathu,
Tizichitano zanu.
(Onaninso Mat. 16:24; Maliko 8:34; Luka 9:23.)