Nyimbo 16
Thawirani ku Ufumu wa Mulungu
(Zefaniya 2:3)
1. Bwerani kwa Yehova ofatsanu,
Zinthu zolungamadi muchite.
Tsiku la Yehova likadzafika
Mwina mungadzabisike.
(KOLASI)
Thawirani ku ’fumu wa M’lungu,
Khalani mbali yake.
N’kumene mudzapeza chitetezo.
M’mvereni, musachedwe.
2. Anjala ya choonadi nonsenu
Mudzamva chisoni mpaka liti?
Bwerani kwa Yehova m’pulumuke
Pansi pa Yesu khalani.
(KOLASI)
Thawirani ku ’fumu wa M’lungu,
Khalani mbali yake.
N’kumene mudzapeza chitetezo.
M’mvereni, musachedwe.
3. Tukulani mitu mosangalala,
Onanitu Ufumu wayamba.
Landirani kuwala kwa Yehova,
Muopeni iye yekha!
(KOLASI)
Thawirani ku ’fumu wa M’lungu,
Khalani mbali yake.
N’kumene mudzapeza chitetezo.
M’mvereni, musachedwe.
(Onaninso Sal. 59:15; Miy. 18:10; 1 Akor. 16:13.)