Nyimbo 24
Yang’ananibe Pamphotho!
(2 Akorinto 4:18)
1. Pomwe akhungu adzaona
Ndipo ogontha adzamvanso,
Pamene madzi adzayenda
Ngakhale muchipululu,
Pomwe wolumala ’dzadumpha,
Abale athu sadzafanso,
Mudzaona madalitsowa
M’kayang’anabe pamphotho.
2. Osalankhula ’dzalankhula,
Okalamba ku unyamata,
Pomwe nthaka idzatulutsa
Zinthu zambiri zabwino,
Pomwe ana ’dzaimba nyimbo,
Kudzakhala mtendere konse,
M’dzaona ’kufa atauka,
M’kayang’anabe pamphotho.
3. Mimbulu idzadya ndi nkhosa,
Zilombo zoopsa ndi ng’ombe.
Mwana adzazitsogolera,
Ndipo zidzamvera iye.
Pamene mantha ndi misozi
Zidzakhala zinthu zakale,
Mudzaona zinthu zonsezi,
M’kayang’anabe pamphotho.
(Onaninso Yes. 11:6-9; 35:5-7; Yoh. 11:24.)