Nyimbo 39
Mtendere Wathu Wamtengo Wapatali
(Yohane 14:27)
1. Tamandani Yehova
Wamtendereyo.
Nkhondo adzazithetsa
Mwa Mwana wake,
Ndipo adzapambana
Nkhondo yabwino
N’kubweretsa mtendere
Padziko lonse.
2. Ukali ndi mkangano,
Izi tasiya.
Mikondo ndi lupanga
Zonse tataya.
Tilitu pa mtendere
Ndi anthu onse.
Monga nkhosa za Yesu,
Ee, zamtendere.
3. Mtendere ndi chipatso
Chachilungamo,
Ndi nzeru yakumwamba,
Yomwe tipempha.
Tiyendebe m’njirayi,
Timaikonda,
Mtendere udzakhala
Padziko lonse.
(Onaninso Sal. 46:9; Yes. 2:4; Yak. 1:17, 18.)