Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 89

Yehova Akutipempha Mokoma Mtima Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzeru”

Yehova Akutipempha Mokoma Mtima Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzeru”

(Miyambo 27:11)

1. Mwana wanga

Undipatse mtima wako

Adzionere yekha

Wonditonzayo.

Nditumikire uli

Wachinyamata,

Onse adziwe kuti

Umandikonda.

(KOLASI)

Mwana wanga wokondedwawe

Khalatu wanzeru chonde.

Usankhe kunditumikira,

Utero ndi mtima wonse.

2. Usangalale ndi

Kunditumikira,

Ngakhale ukapunthwa

Ndidzakudzutsa.

Wina aliyense

Angakulakwire,

Usadere nkhawa

Sindingakusiye.

(KOLASI)

Mwana wanga wokondedwawe

Khalatu wanzeru chonde.

Usankhe kunditumikira,

Utero ndi mtima wonse.

(Onaninso Deut. 6:5; Mlal. 11:9; Yes. 41:13.)