Nyimbo 36
“Chimene Mulungu Wachimanga Pamodzi”
1. Mulungu ndi anthu
Amva malonjezo.
Chingwe cholimba bwino
Chamangidwa lero.
Awa alonjezana
Kuti akondane.
(KOLASI)
‘Chomwe M’lungu wamanga
Musalekanitse.’
2. Cholinga cha M’lungu
Anachifufuza.
Kupeza madalitso
N’komwe akufuna.
Awa agwirizana
Kuti akondane.
(KOLASI)
‘Chomwe M’lungu wamanga
Musalekanitse.’
(Onaninso Gen. 2:24; Mla. 4:12; Aef. 5:22-33.)