Nyimbo 87
Tsopano Ndife Thupi Limodzi
(Genesis 2:23, 24)
1. Fupa la mafupa anga,
Ndiwe mnofu wa mnofu wanga.
M’lungu wandipatsa mnzanga,
Inde wangawanga.
Tsopano tili amodzi,
Yehova ankafuna chonchi.
Monga mwamuna ndi mkazi,
Banja n’limeneli.
Mulungu atitsogolera.
Tsiku ndi tsiku
Chikondi tisonyeza.
Mmene talonjezerana
Zichitike, tizikondana.
Tilemekeze Yehova,
Ndipo ukhalebe wanga.
(Onaninso Gen. 29:18; Mlal. 4:9, 10; 1 Akor. 13:8.)