Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 52

Tetezani Mtima Wanu

Tetezani Mtima Wanu

(Miyambo 4:23)

1. Tetezani mtima wanu

Mukhale ndi moyo.

Mulungu adziwa bwino

Mmene tililidi.

Mtima ndi wonyenga

ungakusocheretseni.

Choncho ganizani bwino,

Mverani Yehova.

2. Konzanitu mtima wanu

Ufune Yehova

Pempherani muuzeni

Za kukhosi kwanu.

Zomwe M’lungu aphunzitsa

Tiyeni timvere,

Choncho tidzamutamanda

Tsiku lililonse.

3. Tetezani mtima wanu

Mupewe zoipa.

Akufikeni pa mtima.

Mawu a Mulungu

Yehova akonda onse

Okhulupirika.

Choncho mulambirenitu

Monga bwenzi lake.

(Onaninso Sal. 34:1; Afil. 4:8; 1 Pet. 3:4.)