Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 102

Tiyeni Tiimbe Nyimbo ya Ufumu!

Tiyeni Tiimbe Nyimbo ya Ufumu!

(Salimo 98:1)

1. Iyi ndi nyimbo yachisangalalo

Yolemekeza M’lungu wamkulu.

Imatipatsadi chiyembekezo,

Imba nafe nyimbo ya Ufumu.

(KOLASI)

‘Lambirani M’lungu wathu,

Mwana waketu ndi mfumu!

Dzaphunzireni nyimbo ya Ufumu

Tamandani dzina la Mulungu.’

2. Ndi nyimboyi tilengeza Ufumu

Khristu Yesu ndi wolamulira.

Ndipo mtundu watsopano wabadwa

Nawo ukumusangalalira.

(KOLASI)

‘Lambirani M’lungu wathu,

Mwana waketu ndi mfumu!

Dzaphunzireni nyimbo ya Ufumu

Tamandani dzina la Mulungu.’

3. Nyimboyi omwe angaiphunzire

Ndi amene amadzichepetsa.

M’dziko lonse ambiri aphunzira.

Akuitananso anthu ena.

(KOLASI)

‘Lambirani M’lungu wathu,

Mwana waketu ndi mfumu!

Dzaphunzireni nyimbo ya Ufumu

Tamandani dzina la Mulungu.’

(Onaninso Sal. 95:6; 1 Pet. 2:9, 10; Chiv. 12:10.)