Nyimbo 75
Tili ndi Zifukwa Zambiri Zokhalira Osangalala
1. Tili ndi zifukwa zambiri
Zakuti tisangalale.
Ndipo anthu m’mayiko onse
Akugwirizana nafe.
Chimwemwe chathu ndi chosatha
Mawu a M’lungu tidziwa.
Iwo amatisangalatsa
Tifuna kuwaphunzira.
Zotisangalatsa n’zambiri
Mumtimamu zikuyaka.
Tikakumana ndi mavuto
Yehova atithandiza.
(KOLASI)
Amatisangalatsadi
Yehova Mulungu wathu.
Iye n’ngwabwino ndi ntchito zake
N’zazikulu ndi zamphamvu.
2. Kumwamba, nyanja ndi dzikoli
N’zosangalatsa kuona.
Yehova analenga zonse,
Kwathu ndi kuyamikira.
Ntchito yochitira umboni
Ikupita patsogolo.
Ufumu ukulamulira
Ubweretsa madalitso.
Kusangalala kwamuyaya
Kwayandikira tsopano.
Zimene anatilonjeza
Tidzasangalala nazo.
(KOLASI)
Amatisangalatsadi
Yehova Mulungu wathu.
Iye n’ngwabwino ndi ntchito zake
N’zazikulu ndi zamphamvu.
(Onaninso Deut. 16:15; Yes. 12:6; Yoh. 15:11.)