Nyimbo 88
Ana Ndi Mphatso Yochokera kwa Mulungu
(Salimo 127:3-5)
1. Mwamuna ’kakhala bambo,
Mkazinso akakhala ndi mwana.
Afunika akumbukire,
Mwanayo siwawo okha.
Ndi mphatso yochoka kwa M’lungu
Amapatsa chikondi ndi moyo.
Amapatsanso malangizo
Othandizadi kwa makolo.
(KOLASI)
Mphatso yanu njopatulika
Ndipo muisamalire.
M’phunzitseni mwana cho’nadi
Choncho mungamuthandize.
2. Malamulo ’nse a M’lungu
Muziwasunga mumtima mwanu.
Muziphunzitsa ana anu,
Uwu ndi udindo wanu.
Muziwaphunzitsa poyenda,
Podzuka ndi pa nthawi yopuma.
Choncho iwo sadzaiwala
Adzakhala odalitsidwa.
(KOLASI)
Mphatso yanu njopatulika
Ndipo muisamalire.
M’phunzitseni mwana cho’nadi
Choncho mungamuthandize.
(Onaninso Deut. 6:6, 7; Aef. 6:4; 1 Tim. 4:16.)