Nyimbo 68
Pemphero la Munthu Wovutika
(Salimo 4:1)
1. Yehova ndapempha:
“Imvani pemphero langa.”
Zilonda zanga zakula
Sizipola msanga.
Kuvutika ndi maganizo
Kwandifoola.
Ndikomereni mtima
Mulungu wotonthoza.
(KOLASI)
Ndidzutseni. Ndichizeni
Nkhawa zanga zichotseni.
Pa mavuto n’thandizeni,
Yehova ndilimbitseni.
2. Ndikafo’ka
Mawu anu amanditonthoza
Kwambiri,
Moti sindingathe kufotokoza.
Ndidziwe kuti,
Chikondi chanu ndi chosatha
Ndiponso n’chachikulu
Kuposa mtima wanga.
(KOLASI)
Ndidzutseni. Ndichizeni
Nkhawa zanga zichotseni.
Pa mavuto n’thandizeni,
Yehova ndilimbitseni.
(Onaninso Sal. 42:6; 119:28; 2 Akor. 4:16; 1 Yoh. 3:20.)