Nyimbo 127
Malo Odziwika ndi Dzina Lanu
(1 Mbiri 29:16)
1. Yehova kukumangirani
Nyumbayi ndi mwayi wathu.
Tikuipereka tsopano
Lidziwike dzina lanu.
Zimene tingakupatseni
Zinalitu kale zanu.
Luso, ntchito ndi chuma chathu
Timakupatsani inu.
(KOLASI)
Tikupereka malowa
Kuti mudziwikedi.
Tikupereka malowa
Chonde alandireni.
2. Tikulemekeza inuyo
Pokutamandani pano,
Landirani ulemerero
Tikamachuluka muno.
Malowa tikukupatsani
Tidzawasamalirabe.
Ndipo apereke umboni
Inde mpaka kalekale.
(KOLASI)
Tikupereka malowa
Kuti mudziwikedi.
Tikupereka malowa
Chonde alandireni.
(Onaninso 1 Maf. 8:18, 27; 1 Mbiri 29:11-14; Mac. 20:24.)