Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 120

Khalani Omvera Kuti Mulandire Madalitso

Khalani Omvera Kuti Mulandire Madalitso

(Luka 11:28)

1. Kodi ndife anthu omvera Khristu

Pa zonse zimene ananena?

Kuzidziwa n’kosangalatsa ndithu.

Tidalitsidwa tikazimvera.

(KOLASI)

Mvera udalitsidwe

Kuti usangalale.

Zomwe Mulungu angakuuze

Mvera udalitsidwe.

2. Monga nyumba yomangidwa pathanthwe

Osati yomangidwa pamchenga,

Zochita zathu zingatiteteze

Kokha ngati Yesu timumvera.

(KOLASI)

Mvera udalitsidwe

Kuti usangalale.

Zomwe Mulungu angakuuze

Mvera udalitsidwe.

3. Monga mtengo wamumbali mwa madzi

Umabereka nthawi ’kafika,

Tikamvera tidzadalitsidwadi

Moyo wosatha tidzalandira.

(KOLASI)

Mvera udalitsidwe

Kuti usangalale.

Zomwe Mulungu angakuuze

Mvera udalitsidwe.

(Onaninso Deut. 28:2; Sal. 1:3; Miy. 10:22; Mat. 7:24-27.)