Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 90

Ulemerero Umene Umabwera Chifukwa cha Imvi

Ulemerero Umene Umabwera Chifukwa cha Imvi

(Miyambo 16:31)

1. Pakati pathu pali

Achikulire.

Akukondabe M’lungu

Sanamusiye.

Ena imfa ya mnzawo

Ikuwawawa.

Tate atonthozeni,

N’kuwalimbitsa.

(KOLASI)

Mumakumbukira

Zochita zawo.

Tate auzeni:

“Mwachita bwino.”

2. Imvi za olungama

Ndi zokongola.

Zimasangalatsadi

Tate Yehova.

Ife tikumbukire

Pa nthawi ina

Pa unyamata wawo

Ankayesetsa.

(KOLASI)

Mumakumbukira

Zochita zawo.

Tate auzeni:

“Mwachita bwino.”

(Onaninso Sal. 71:9, 18; Miy. 20:29; Mat. 25:21, 23; Luka 22:28; 1 Tim. 5:1.)