Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 66

Tizitumikira Yehova ndi Moyo Wathu Wonse

Tizitumikira Yehova ndi Moyo Wathu Wonse

(Mateyu 22:37)

1. Yehova Wamphamvuyonse

Inetu ndimakukondani.

Mtima wanga wonse umafuna

Kukutumikirani.

Malamulo anu ndimvera

Zofuna zanu ndichita.

(KOLASI)

Inu Yehova ndinu woyenera

Kutumikiridwa.

2. Atate, zomwe munalenga

Zimakulemekezani.

Ndadzipereka ndi mphamvu

Zonse kukutumikirani.

Zonse ndinakulonjezani

Ndidzayesetsa kuchita.

(KOLASI)

Inu Yehova ndinu woyenera

Kutumikiridwa.

(Onaninso Deut. 6:15; Sal. 40:8; 113:1-3; Mlal. 5:4; Yoh. 4:34.)