Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 112

Yehova, Mulungu Wamkulu

Yehova, Mulungu Wamkulu

(Ekisodo 34:6, 7)

1. Inu Yehova M’lungu wamkulu

Ndinu woyeneradi

Kutamandidwa zedi.

Ndinu wabwino ndi wolungama.

Ndinu M’lungu kosatha.

2. Mumakhululukiradi anthu

Amene monga inu

Ndi achifundo ndithu.

Mumasonyeza kukoma mtima

Pa zonse mumachita.

3. Mutamandidwe ndi anthu onse

Dzina lanu liyere

Wina asalikane.

Dziko lapansi likhale mmene

Inu mumafunira.

(Onaninso Deut. 32:4; Miy. 16:12; Mat. 6:10; Chiv. 4:11.)