Nyimbo 79
Kukoma Mtima Ndi Khalidwe Lofunika Kwambiri
(Aefeso 4:32)
1. Tikuthokoza chifukwa choti
Yehova tam’dziwa.
Ngakhale n’ngwanzeru ndi wamphamvu,
Iye ndi wokoma mtima.
2. Yesu akuitana otopa
Awatsitsimule.
Ndipo goli lake ndi lofewa
Chifukwa n’ngokoma mtima.
3. Mulungu komanso Mbuye Yesu
Tiziwatsanzira.
M’zochita zathu tifunikira
Kukhala okoma mtima.
(Onaninso Mika 6:8; Mat. 11:28-30; Akol. 3:12; 1 Pet. 2:3.)