Nyimbo 129
Tigwire Mwamphamvu Chiyembekezo Chathu
(Aheberi 6:18, 19)
1. Anthu akhala akuyenda mumdima
Ndipo sanapindule kanthu n’komwe.
Zadziwika kuti anthu ochimwa
Kuvutika sangakuchotse.
(KOLASI)
Tiyeni tiimbe mokondwera
Poti Ufumu wa M’lungu wafika!
Yesu adzachotsadi zoipa,
Chiyembekezochi n’chonga nangula.
2. Uthenga womwe ukumveka ndi woti:
“Tsiku la Mulungu layandikira.”
Anthu ake sadzamvanso chisoni
M’lungu wathu timuimbira.
(KOLASI)
Tiyeni tiimbe mokondwera
Poti Ufumu wa M’lungu wafika!
Yesu adzachotsadi zoipa,
Chiyembekezochi n’chonga nangula.
(Onaninso Hab. 1:2, 3; Sal. 27:14; Yow. 2:1; Aroma 8:22.)