Nyimbo 121
Tizilimbikitsana
(Aheberi 10:24, 25)
1. Pomwe timalimbikitsana
Kutumikira Yehova
Timakhaladi okondana
Komanso ogwirizana.
Chikondi cha anthu a M’lungu
Chimatipatsadi mphamvu.
Kumene tingatetezeke
Ndi mkati mwa mpingo wathu.
2. Mawu ochoka kwa abale
A pa nthawi yoyenera
Ndi olimbikitsa kwambiri
Ndipo amatitonthoza.
Kugwirira ntchito limodzi
Ndithu ndikosangalatsa,
Timafuna kuthandizana
Ndi kumalimbikitsana.
3. Popeza tsiku la Yehova
Layandikira kwambiri
Ndikofunika tisaleke
Kusonkhanatu pamodzi.
Tikufuna kutumikira
Ndi abale kwamuyaya.
Choncho ndi njira yachikondi
Kuti tizithandizana.
(Onaninso Luka 22:32; Mac. 14:21, 22; Agal. 6:2; 1 Ates. 5:14.)