Nyimbo 58
Pemphero Langa Losonyeza Kudzipereka
1. Tengani mtima wanga
Cho’nadi uzikonda.
Maganizo tengani
Ndikutumikireni.
2. Manja anga tengani
Akutumikireni.
Tengani mawu anga,
Ndi’mbire Mfumu yanga.
3. Moyo wanga mu’tenge,
Zabwino ndizichite.
Yehova nditengeni,
Ndikusangalatseni.
(Onaninso Sal. 40:8; Yoh. 8:29; 2 Akor. 10:5.)