Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 95

“Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino”

“Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino”

(Salimo 34:8)

1. Kutumikira Mulungu

Kumatisangatsadi.

Ntchito n’njambiri yolalikira

Timaipezera nthawi.

(KOLASI)

M’lungu akuti: ‘Talawani,

Inetu ndi wabwino’

Timapindula tikachita

Zonse zomwe tingathe.

2. Mtumiki wanthawi zonse

M’lungu amamudalitsa.

Amalandira zosowa zake

Amakhala wokhutira.

(KOLASI)

M’lungu akuti: ‘Talawani,

Inetu ndi wabwino’

Timapindula tikachita

Zonse zomwe tingathe.

(Onaninso Maliko 14:8; Luka 21:2; 1 Tim. 1:12; 6:6.)