Nyimbo 124
Alandireni Bwino
(Machitidwe 17:7)
1. Yehova ndi M’lungu wopanda tsankho
Amapatsa onse zofuna zawo.
Amapatsa dzuwa
Ngakhalenso mvula
Amatisangalatsa mtima.
Osauka tikamawathandiza.
Mulungu wathu tidzamutsanzira,
Adzatidalitsa tikamachitira
Ena zinthu mokoma mtima.
2. Pothandiza ena sitingadziwe
Madalitso omwe tingalandire.
Angakhale anthu achilendo ndithu,
Tiwapatse zosowa zawo.
Monga Lidiya wa m’nthawi yakale,
Akabwera kwathu tiwalandire.
M’lungu amadziwa
onse om’tsanzira
Pochitira ena chifundo.
(Onaninso Mac. 16:14, 15; Aroma 12:13; 1 Tim. 3:2; Aheb. 13:2; 1 Pet. 4:9.)