Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 96

Fufuzani Anthu Oyenerera

Fufuzani Anthu Oyenerera

(Mateyu 10:11-15)

1. Ambuye wathu anatisonyeza

Njira yolalikirira:

‘Kulikonse kumene mungapite

Fufuzani oyenerera.

Muziwapatsa moni eni nyumba

Ndikuwafunira mtendere.

Ngati akana sansani fumbi

Kumapazi anu muwasiye.’

2. Onse amene akulandirani

Alandiranso Ambuye.

Mulungu adzawathandizadi

Kuti nawonso atumikire.

Musade nkhawa kuti munenanji,

Yehova adzakuuzani.

Ngati mutayankha mokoma mtima

Ofatsa adzakumverani.

(Onaninso Mac. 13:48; 16:14; Akol. 4:6.)