Nyimbo 69
Ndidziwitseni Njira Zanu
(Salimo 25:4)
1. Yehova tasonkhanatu pamodzi
Pomvera kuitana kwanu.
Mawu anu ndi nyale m’njira yathu,
Amatiphunzitsa za inu.
(KOLASI)
Ndiphunzitseni njira zanuzo
Ndikhale womvera malamulo.
Ndiyendetseni m’njira yoona
Malamulo anu ndizikonda.
2. Nzeru zanu Yehova ndi zakuya,
Mfundo zanu n’zolimbikitsa.
Mawu anu adzakhala kosatha,
Timapezamo zodabwitsa.
(KOLASI)
Ndiphunzitseni njira zanuzo
Ndikhale womvera malamulo.
Ndiyendetseni m’njira yoona
Malamulo anu ndizikonda.
(Onaninso Eks. 33:13; Sal. 1:2; 119:27, 35, 73, 105.)