Nyimbo 57
Kusinkhasinkha kwa Mtima Wanga
(Salimo 19:14)
1. Zomwe ndimasinkhasinkha,
Zimene ndimaganiza,
Zikukondweretseni Ya
Kuti ndikhale wolimba.
Pamene ndili ndi nkhawa
N’kumalephera kugona
Ndisinkhesinkhe za inu,
Inde zinthu zoyenera.
2. Zilizonse zolungama,
Zofunika ndi zoona,
Ndikamaziganizira
Zindipezetse mtendere.
Nzeru zanu n’zofunika
Komanso ndi zochuluka.
Choncho ndizisinkhasinkha
Zonena zanu mwakhama.
(Onaninso Sal. 49:3; 63:6; 139:17, 23; Afil. 4:7, 8; 1 Tim. 4:15.)