Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Nyimbo 119

Bwerani Mudzatsitsimulidwe!

Bwerani Mudzatsitsimulidwe!

(Aheberi 10:24, 25)

1. Tikukhaladi m’dziko losochera,

Anthu sakudziwa M’lungu.

Tikufunikiradi malangizo

Osonyeza njira yathu.

Misonkhano yathu imathandiza

Kukhala n’chiyembekezo,

Imatilimbikitsa n’kutipatsa

Mphamvu yochita zabwino.

Zimene Yehova watilamula

Ife sitidzazisiya.

Pamisonkhano yathu timapeza

Malangizo oyenera.

2. Yehova akudziwa bwino zinthu

Zomwe timafunikira.

Tikamasonkhana timasonyeza

Kuti timamudalira.

Tikamamvera nkhani za abale

Timalimbikitsidwadi.

Timadziwa kuti sitili tokha,

Iwo atithandizadi.

Poyembekezera Paradaiso

Sitisiya kusonkhana.

Tiziphunzira kugwiritsa ntchito

Nzeru yochoka kumwamba.

(Onaninso Sal. 37:18; 140:1; Miy. 18:1; Aef. 5:16; Yak. 3:17.)