Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Oyamba

Mawu Oyamba

Kodi zamoyo zinachita kulengedwa kapena zinangokhalapo zokha? Anthu ambiri ali ndi maganizo osiyanasiyana pa nkhaniyi. Koma kudziwa zoona zake n’kofunika kwambiri. Kabukuka kamayankha mafunso ngati awa:

  • Kodi dzikoli linapangidwa kuti muzikhala zamoyo?

  • Kodi tingaphunzire chiyani pa zinthu za m’chilengedwe?

  • Kodi zimene anthu amaphunzitsa zoti zamoyo zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina zili ndi umboni wake?

  • Kodi sayansi imasonyeza kuti nkhani ya m’Baibulo yokhudza kulenga zinthu si yoona?

  • Kodi zimene mumakhulupirira pa nkhaniyi zimakhudza bwanji moyo wanu?