GAO 5
Cigumula ca Nowa—Ndani Anamvetsela? Ndani Sanamvetsele?
Anthu ambili m’nthawi ya Nowa anali kucita zoipa. Genesis 6:5
Adamu ndi Hava anabala ana, ndipo anthu anaculuka padziko lapansi. M’kupita kwa nthawi, angelo ena anapanduka ndi kugwilizana ndi Satana.
Iwo anabwela padziko lapansi ndi kuvala matupi a anthu kuti akwatile akazi. Akazi amenewa anabala viŵana vikulu-vikulu vimene vinali vamphamvu ndi voopsa.
Dziko linadzala ndi anthu amene anali kucita zoipa. Baibo imakamba kuti: ‘Kuipa kwa anthu kunaculuka padziko lapansi, ndipo malingalilo onse a m’mitima ya anthu anali oipa okha-okha nthawi zonse.’
Genesis 6:13, 14, 18, 19, 22
Nowa anamvetsela kwa Mulungu ndi kumanga cingalawa.Nowa anali munthu wabwino. Yehova anauza Nowa kuti adzaononga anthu oipa ndi cigumula cacikulu.
Mulungu anauza Nowa kumanga ciboti cacikulu cochedwa cingalawa, ndi kuloŵetsamo banja lake ndi nyama zosiyana-siyana.
Nowa anacenjeza anthu za Cigumula cimene cinali kubwela, koma iwo sanamvele. Ena anam’seka; ena anam’zonda.
Pamene Nowa anatsiliza kumanga cingalawa, analoŵetsamo nyama.