Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

PHUNZIRO 6

Kodi Timapindula Bwanji Tikamasonkhana ndi Akhristu Anzathu?

Kodi Timapindula Bwanji Tikamasonkhana ndi Akhristu Anzathu?

Madagascar

Norway

Lebanon

Italy

Nthawi zonse timapita kumisonkhano yachikhristu, ngakhale kuti nthawi zina nyengo imakhala yoipa kwambiri kapena tingafunike kudutsa m’nkhalango yowirira kwambiri. A Mboni za Yehova amaonetsetsa kuti akasonkhane ndi Akhristu anzawo ngakhale kuti amakumana ndi mavuto osiyanasiyana komanso nthawi zina amakhala atatopa pambuyo poweruka kuntchito. N’chifukwa chiyani iwo amachita zimenezi?

Kusonkhana ndi anzathu kumatithandiza kuti zinthu zizitiyendera bwino. Pa nthawi ina, Paulo ananena kuti “tiyeni tiganizirane.” Iye ananena zimenezi posonyeza zimene tiyenera kuchita ndi anthu amene timasonkhana nawo kumpingo. (Aheberi 10:24) Mawu amenewa akutanthauza kuti tiyenera kudziwana bwino ndi ena kapena kuwamvetsa bwino. Choncho mawu a mtumwi Paulo amenewa akutilimbikitsa kuti tiyenera kuganizira ena. Tikamayesetsa kudziwana bwino ndi mabanja ena achikhristu, tikhoza kudziwa zimene achita polimbana ndi mavuto ofanana ndi athu ndipo angatithandize kuti nafenso tithane ndi mavuto athuwo.

Timalimbitsa ubwenzi wathu ndi anzathu. Sikuti anthu amene timasonkhana nawo ndi ongodziwana nawo chabe koma ndi anzathu apamtima. Nthawi zina timachitira limodzi zosangalatsa zina. Kodi zimenezi zili ndi phindu lanji? Zimenezi zimathandiza kuti tikhale ndi mtima woyamikira kwambiri Akhristu anzathu, ndipo mtima umenewu umatithandiza kuti tizikondana kwambiri. Komanso, pamene anzathu akukumana ndi mavuto, timakhala okonzeka kuwathandiza chifukwa cha ubwenzi wolimba umene ulipo. (Miyambo 17:17) Tikamasonkhana ndi mpingo komanso kuchitira pamodzi zinthu zina ndi Akhristu anzathu, timasonyeza kuti ‘tikusamalirana mofanana.’​—1 Akorinto 12:25, 26.

Tikukulimbikitsani kuti musankhe anthu amene akuchita chifuniro cha Mulungu kuti akhale mabwenzi anu. Anthu oterewo mungawapeze pakati pa Mboni za Yehova. Musalole kuti chilichonse chikulepheretseni kusonkhana nafe.

  • Kodi timapeza madalitso otani tikamasonkhana ndi anzathu?

  • Kodi mubwera liti kumisonkhano yathu kuti mudzadziwane bwino ndi anthu a mumpingo mwathu?