Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

PHUNZIRO 25

N’chifukwa Chiyani Timamanga Nyumba za Ufumu Ndipo Timazimanga Bwanji?

N’chifukwa Chiyani Timamanga Nyumba za Ufumu Ndipo Timazimanga Bwanji?

Bolivia

Nigeria, nyumba yakale komanso yatsopano

Tahiti

Mfundo yaikulu ya m’Baibulo imene timaphunzira ku Nyumba ya Ufumu ndi yokhudzana ndi Ufumu wa Mulungu. Ndipotu mfundo yaikulu pa utumiki wa Yesu inali yokhudzanso Ufumu wa Mulungu.​—Luka 8:1.

Ndi malo amene anthu amalambira Mulungu m’njira yovomerezeka. Ku Nyumba ya Ufumu n’kumene Mboni za Yehova zimakonzekera ntchito yolalikira uthenga wabwino m’deralo. (Mateyu 24:14) Kukula kwa Nyumba za Ufumu komanso kamangidwe kake kamakhala kosiyanasiyana. Komabe, zonse zimakhala zooneka bwino ndipo nyumba zambiri zimagwiritsidwa ntchito ndi mipingo ingapo. M’zaka za posachedwapa tamanga Nyumba za Ufumu zambirimbiri (tinganene kuti padziko lonse tinkamanga nyumba zisanu tsiku lililonse). Izi zachitika chifukwa chakuti mipingo ikuwonjezeka kwambiri. Kodi zatheka bwanji kuti timange nyumba zochuluka choncho?​—Mateyu 19:26.

Nyumbazi zimamangidwa pogwiritsa ntchito ndalama zimene zimaperekedwa ku thumba lapadera. Zopereka zimenezi zimatumizidwa kuofesi ya Mboni za Yehova kuti zikaperekedwe ku mipingo imene ikufuna kumanga kapena kukonzanso Nyumba za Ufumu.

Nyumba za Ufumu zimamangidwa ndi anthu osiyanasiyana ongodzipereka omwe salipiridwa. M’mayiko ambiri muli Magulu Omanga Nyumba za Ufumu. Abale ndi alongo amene amagwira ntchito mongodzipereka m’magulu amenewa amapita m’mipingo yosiyanasiyana m’dziko lomwelo. Iwo amakafika kumadera akumidzi kuti akathandize pa ntchito yomanga Nyumba ya Ufumu komanso kuphunzitsa abale a kumeneko mmene angagwirire ntchitoyi. M’mayiko ena muli abale omwe amayang’anira ntchito yomanga ndi kukonzanso Nyumba za Ufumu m’gawo limene apatsidwa. Akulu amene amadziwa bwino ntchito ya zomangamanga amatsogolera mipingo pomanga Nyumba za Ufumu ndipo amaonetsetsa kuti zonse zimene zimafunika pa ntchitoyi zachitika. Pamakhala amisiri odziwa ntchito zosiyanasiyana, omwe amadzipereka pa ntchito imeneyi. Ngakhale kuti anthu ambiri amene amathandizira pa ntchitoyi mongodzipereka, amakhala a mumpingo momwemo. Zonsezi zikutheka chifukwa chakuti Yehova akutithandiza ndi mzimu wake komanso anthu ake akugwira ntchitoyi modzipereka.​—Salimo 127:1; Akolose 3:23.

  • N’chifukwa chiyani malo athu olambirira amatchedwa Nyumba ya Ufumu?

  • Kodi zimatheka bwanji kumanga Nyumba za Ufumu padziko lonse?