Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

PHUNZIRO 28

Kodi Pamalo Athu a pa Intaneti Pali Zinthu Zotani?

Kodi Pamalo Athu a pa Intaneti Pali Zinthu Zotani?

France

Poland

Russia

Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Onetsani kuwala kwanu pamaso pa anthu, kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kuti alemekeze Atate wanu wakumwamba.” (Mateyu 5:16) Kuti tikwanitse kuchita zimenezi, tikugwiritsa ntchito zinthu zamakono monga Intaneti. Pawebusaiti yathu ya jw.org, pamapezeka nkhani zofotokoza zimene ife a Mboni za Yehova timakhulupirira komanso zimene timachita. Kodi Pawebusaiti Yathu Pali Zinthu Zotani?

Pamapezeka mayankho a m’Baibulo a mafunso amene anthu amakonda kufunsa. Mungapezepo mayankho a mafunso ofunika kwambiri amene anthu amakonda kufunsa. Mwachitsanzo kapepala kakuti, Kodi Mavuto Amene Tikukumana Nawowa Adzathadi?, ndi kakuti Kodi N’zoonadi Kuti Akufa Adzauka?, timapezeka pawebusaitiyi m’zinenero zoposa 600. Mungapezeponso Baibulo la Dziko Latsopano m’zinenero zoposa 130 komanso mabuku angapo othandiza pophunzira Baibulo monga buku lakuti, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? Ndiponso mungapezepo magazini atsopano a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Mungawerenge kapena kumvetsera pa Intaneti mabuku ndi magazini amenewa. Mungathenso kuzichotsa pa Intaneti n’kuziika pa kompyuta kapena pachipangizo china kuti muzimvetsera kapena kuwerenga. Mukhozanso kusindikiza masamba ena ochepa a buku kapena magazini imene mwapeza pa Intaneti n’cholinga choti mukapatse munthu wina wachidwi m’chinenero chake. Palinso mavidiyo a m’zinenero zamanja zambiri. Mungapange dawunilodi nkhani za m’Baibulo zomwe zinajambulidwa mwasewero, mavidiyo a masewero a nkhani za m’Baibulo komanso nyimbo zosangalatsa zomwe mungamvetsere nthawi ina iliyonse.

Pali nkhani zofotokoza bwino mmene mpingo wa Mboni za Yehova ulili. Chinanso chomwe chimapezeka pawebusaiti yathu ndi nkhani zaposachedwapa zokhudza Mboni za Yehova ndi mavidiyo osonyeza zinthu zokhudza ntchito yapadziko lonse komanso mmene timathandizirana pakagwa tsoka. Mungapezenso masiku amene misonkhano ikuluikulu idzachitike, komanso maadiresi kapena manambala a foni a maofesi osiyanasiyana a Mboni za Yehova.

Chifukwa cha zinthu ngati zimenezi tikuonetsa kuwala kwa choonadi ngakhale kumadera akutali kwambiri. Anthu padziko lonse lapansi ngakhale kumadera akutali ngati ku Antarctica, akuphunzira choonadi cha m’Baibulo. Tikupemphera kuti “mawu a Yehova apitirize kufalikira mofulumira” padziko lonse lapansi n’cholinga choti Mulungu alemekezedwe.​—2 Atesalonika 3:1.

  • Kodi webusaiti yathu ya jw.org ikuthandiza bwanji anthu kuphunzira choonadi cha m’Baibulo?

  • Kodi mungakonde kufufuza zinthu zotani pawebusaiti yathu?