Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Nyimbo 142

Tizilalikira kwa Anthu a Mitundu Yonse

Tizilalikira kwa Anthu a Mitundu Yonse

(1 Timoteyo 2:4)

  1. Timutsanzire Mulungu wathu

    Pokhala anthu opanda tsankho.

    Akufuna kuti anthu onse,

    Amve uthenga, apulumuke.

    (KOLASI)

    Wofunika ndi munthu,

    Osati mtundu wake.

    Tiphunzitse onse mosasankha

    Timakondatu anthu,

    Tiwauze uthenga

    ‘Akhale mabwenzi a Yehova.’

  2. Kulikonse angapezekeko,

    Kaya akuoneka motani,

    Mtima wawo ndiwo wofunika.

    Yehova amaona mtimawo.

    (KOLASI)

    Wofunika ndi munthu,

    Osati mtundu wake.

    Tiphunzitse onse mosasankha

    Timakondatu anthu,

    Tiwauze uthenga

    ‘Akhale mabwenzi a Yehova.’

  3. Yehova amalandira anthu

    Omwe asankha kum’tumikira.

    Choncho anthu a mitundu yonse,

    Tiwauze uthenga wabwino.

    (KOLASI)

    Wofunika ndi munthu,

    Osati mtundu wake.

    Tiphunzitse onse mosasankha

    Timakondatu anthu,

    Tiwauze uthenga

    ‘Akhale mabwenzi a Yehova.’