Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

GAWO 1

Zimene Zinachitika Yesu Asanayambe Utumiki Wake

“Ameneyu adzakhala wamkulu.”—Luka 1:32

Zimene Zinachitika Yesu Asanayambe Utumiki Wake

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 1

Mauthenga Awiri Ochokera kwa Mulungu

Mngelo Gabirieli anapereka mauthenga ovuta kuwakhulupirira.

MUTU 2

Yesu Analemekezedwa Asanabadwe

Kodi Elizabeti komanso mwana amene anali m’mimba mwake analemekeza bwanji Yesu?

MUTU 3

Kubadwa kwa Wokonza Njira

Zekariya atayambiranso kulankhula ananena ulosi wofunika kwambiri.

MUTU 4

Mariya Anakhala ndi Pakati Asanakwatiwe

Kodi Yosefe anakhulupirira zimene Mariya anamuuza kuti anali ndi pakati, chifukwa cha mzimu woyera osati chifukwa chakuti anagona ndi mwamuna wina?

MUTU 5

Kodi Yesu Anabadwa Liti Ndipo Anabadwira Kuti?

Kodi timadziwa bwanji kuti Yesu sanabadwe pa 25 December?

MUTU 6

Mwana Amene Mulungu Analonjeza

Yosefe ndi Mariya atapita ndi Yesu kukachisi, Aisiraeli awiri omwe anali achikulire ananeneratu zimene Yesu adzachite m’tsogolo.

MUTU 7

Okhulupirira Nyenyezi Anapita Kukaona Yesu

N’chifukwa chiyani nyenyezi imene inatsogolera anthu a kum’mawa inayamba kuwatsogolera kwa mfumu yankhanza Herode, m’malo mowatsogolera kwa Yesu?

MUTU 8

Anathawa Mfumu Yankhanza

Maulosi atatu a m’Baibulo onena za Mesiya anakwaniritsidwa Yesu akadali mwana.

MUTU 9

Yesu Anakulira Ku Nazareti

Kodi Yesu anali ndi achimwene ndi achemwali angati?

MUTU 10

Yosefe ndi Banja Lake Anapita ku Yerusalemu

Yosefe ndi Mariya anavutika kwambiri Yesu atasowa, pomwe Yesuyo anadabwa kwambiri kuti makolo ake samadziwa kumene akanamupeza.

MUTU 11

Yohane M’batizi Anakonza Njira

Afarisi ndi Asaduki atapita kwa Yohane, iye anawadzudzula. N’chifukwa chiyani anachita zimenezi?