GAWO 1
Zimene Zinachitika Yesu Asanayambe Utumiki Wake
“Ameneyu adzakhala wamkulu.”—Luka 1:32
M'CHIGAWO ICHI
MUTU 1
Mauthenga Awiri Ochokera kwa Mulungu
Mngelo Gabirieli anapereka mauthenga ovuta kuwakhulupirira.
MUTU 2
Yesu Analemekezedwa Asanabadwe
Kodi Elizabeti komanso mwana amene anali m’mimba mwake analemekeza bwanji Yesu?
MUTU 4
Mariya Anakhala ndi Pakati Asanakwatiwe
Kodi Yosefe anakhulupirira zimene Mariya anamuuza kuti anali ndi pakati, chifukwa cha mzimu woyera osati chifukwa chakuti anagona ndi mwamuna wina?
MUTU 5
Kodi Yesu Anabadwa Liti Ndipo Anabadwira Kuti?
Kodi timadziwa bwanji kuti Yesu sanabadwe pa 25 December?
MUTU 6
Mwana Amene Mulungu Analonjeza
Yosefe ndi Mariya atapita ndi Yesu kukachisi, Aisiraeli awiri omwe anali achikulire ananeneratu zimene Yesu adzachite m’tsogolo.
MUTU 7
Okhulupirira Nyenyezi Anapita Kukaona Yesu
N’chifukwa chiyani nyenyezi imene inatsogolera anthu a kum’mawa inayamba kuwatsogolera kwa mfumu yankhanza Herode, m’malo mowatsogolera kwa Yesu?
MUTU 8
Anathawa Mfumu Yankhanza
Maulosi atatu a m’Baibulo onena za Mesiya anakwaniritsidwa Yesu akadali mwana.
MUTU 10
Yosefe ndi Banja Lake Anapita ku Yerusalemu
Yosefe ndi Mariya anavutika kwambiri Yesu atasowa, pomwe Yesuyo anadabwa kwambiri kuti makolo ake samadziwa kumene akanamupeza.
MUTU 11
Yohane M’batizi Anakonza Njira
Afarisi ndi Asaduki atapita kwa Yohane, iye anawadzudzula. N’chifukwa chiyani anachita zimenezi?