GAWO 3
Yesu Analalikira Kwambiri ku Galileya
‘Yesu anayamba kulalikira kuti: “Ufumu wakumwamba wayandikira.”’—Mateyu 4:17
M'CHIGAWO ICHI
MUTU 20
Chozizwitsa Chachiwiri Chimene Yesu Anachita Ku Kana
Yesu anachiritsa mwana yemwe anali pamtunda wa makilomita 26.
MUTU 21
Zimene Zinachitika Yesu Ali ku Sunagoge wa ku Nazareti
Kodi Yesu ananena chiyani kuti anthu a m’tauni ya kwawo afike pofuna kumupha?
MUTU 23
Yesu Anachita Zozizwitsa Ali ku Kaperenao
Pamene Yesu ankatulutsa mizimu yoipa, n’chifukwa chiyani analetsa mizimuyo kuti isawuze anthu kuti iyeyo ndi Mwana wa Mulungu?
MUTU 24
Yesu Analalikira M’madera Ambiri a ku Galileya
Anthu anapita kwa Yesu kuti akachiritsidwe, komabe Yesu anafotokoza kuti utumiki wake unali ndi cholinga chinachake chapadera.
MUTU 25
Yesu Anachitira Chifundo Munthu Wakhate N’kumuchiritsa
Yesu analankhula mawu ochepa koma amphamvu kwambiri ndipo zimene analankhulazo zinasonyeza kuti ankaganizira anthu amene ankawachiritsa.
MUTU 26
“Machimo Ako Akhululukidwa”
Kodi Yesu anasonyeza kuti pali kugwirizana kotani pakati pa uchimo ndi matenda?
MUTU 28
N’chifukwa Chiyani Ophunzira a Yesu Sankasala Kudya?
Poyankha Yesu anafotokoza fanizo la matumba a chikopa.
MUTU 29
Kodi Kunali Kulakwa Kugwira Ntchito Yabwino pa Sabata?
N’chifukwa chiyani Ayuda ankavutitsa Yesu atachiritsa munthu amene ankadwala kwa zaka 38?
MUTU 30
Kodi Pali Ubale Wotani Pakati pa Yesu ndi Mulungu?
Ayuda ankaganiza kuti Yesu ankadziona kuti ndi wofanana ndi Mulungu, koma Yesu anafotokoza kuti Mulungu ndi wamkulu kwa iyeyo.
MUTU 31
Anabudula Ngala za Tirigu pa Tsiku la Sabata
N’chifukwa chiyani Yesu ananena kuti iye ndi “Mbuye wa Sabata”?
MUTU 32
Kodi Malamulo Ankalola Munthu Kuchita Chiyani pa Sabata?
Nthawi zambiri Asaduki ndi Afarisi sankagwirizana koma anagwiriza n’cholinga choti atsutse Yesu.
MUTU 33
Ulosi wa Yesaya Unakwaniritsidwa
N’chifukwa chiyani Yesu ankauza anthu amene wawachiritsa kuti asamauze anthu ena zimene wachita komanso kuti iye ndi ndani?
MUTU 35
Ulaliki Wotchuka wa Paphiri
Werengani nkhaniyi kuti mudziwe mfundo zofunika kwambiri zimene Yesu anaphunzitsa.
MUTU 36
Kapitawo wa Asilikali Anasonyeza Kuti Anali ndi Chikhulupiriro
Kodi kapitawo wa asilikali anachita chiyani chomwe chinadabwitsa Yesu?
MUTU 37
Yesu Anaukitsa Mwana Wamwamuna wa Mzimayi Wamasiye
Anthu amene anaona Yesu akuukitsa mnyamatayo anamvetsa tanthauzo lake.
MUTU 38
Yohane Yemwe Anali M’ndende Ankafuna Kumva Kuchokera kwa Yesu
N’chifukwa chiyani Yohane m’batizi anafunsa ngati Yesu analidi Mesiya? Kodi Yohane ankakayikira?
MUTU 39
Tsoka kwa M’badwo Umene Sunamvere
Yesu ananena kuti chilango cha Sodomu pa Tsiku la Chiweruzo chidzakhala chocheperako poyerekeza ndi cha Kaperenao. Ku Kaperenao n’kumene Yesu ankakhala nthawi zambiri.
MUTU 40
Anawaphunzitsa Kukhululukira Ena
Kodi pamene Yesu anauza mzimayi yemwe mwina anali hule kuti machimo ake akhululukidwa, ankatanthauza kuti palibe vuto lililonse ngati munthu atachita zinthu zosiyana ndi malamulo a Mulungu?
MUTU 41
Kodi Yesu Ankazitenga Kuti Mphamvu Zochitira Zozizwitsa?
Abale ake a Yesu ankaganiza kuti wachita misala.
MUTU 44
Yesu Analetsa Mphepo Yamphamvu Panyanja
Zimene Yesu anachita poletsa mphepo ndi mafunde pa nyanja zimasonyeza mmene moyo udzakhalire akadzayamba kulamulira monga Mfumu.
MUTU 46
Anachira Atagwira Malaya a Yesu
Yesu anasonyeza kuti anali wachifundo komanso kuti anali ndi mphamvu pamene anachiritsa mzimayi wodwala matenda otaya magazi.
MUTU 47
Kamtsikana Kanakhalanso ndi Moyo
Yesu atanena kuti mtsikana womwalirayo akugona anthu anayamba kuseka kwambiri. Kodi anthuwo sankadziwa kuti Yesu akhoza kuchita chiyani?
MUTU 48
Yesu Anachita Zozizwitsa Koma Anakanidwa Ngakhale Kwawo ku Nazareti
Anthu a ku Nazareti anakana Yesu, osati chifukwa cha zozizwitsa kapena zimene ankaphunzitsa, koma anali ndi zifukwa zina.
MUTU 49
Analalikira ku Galileya Komanso Anaphunzitsa Atumwi
Kodi mawu akuti ‘Ufumu wakumwamba wayandikira’ ankatanthauza chiyani?
MUTU 50
Anawakonzekeretsa Kuti Azilalikira Ngakhale Pamene Akuzunzidwa
Popeza atumwi sankafunika kuopa imfa, n’chifukwa chiyani Yesu anawauza kuti adzathawe akamadzazunzidwa?
MUTU 51
Anaphedwa pa Tsiku Lokondwerera Kubadwa
Salome anasangalatsa Herode ndi mmene anavinira moti Herode anamulonjeza kuti amupatsa chilichonse chimene angapemphe. Kodi Salome anapempha chiyani?
MUTU 52
Anadyetsa Anthu Masauzande Ambiri ndi Mikate Komanso Nsomba Zochepa
Chozizwitsa chimene Yesu anachita pa nthawi imeneyi chinali chapadera kwambiri moti chinalembedwa m’Mauthenga onse 4.
MUTU 53
Wolamulira Amene Akhoza Kulamulira Mphepo Yamphamvu
Kodi atumwi anazindikira chiyani ataona Yesu akuyenda pamadzi komanso ataletsa mphepo yamphamvu?
MUTU 54
Yesu Ndiye “Chakudya Chopatsa Moyo”
N’chifukwa chiyani Yesu anadzudzula anthu ngakhale kuti anayesetsa kumufunafuna kuti amupeze?
MUTU 55
Kudya Mnofu wa Yesu ndi Kumwa Magazi Ake
Yesu anaphunzitsa zinthu zimene zinadabwitsa ophunzira ake moti ambiri anasiya kumutsatira.
MUTU 56
Kodi Chimaipitsa Munthu N’chiyani?
Kodi chimaipitsa munthu n’chiyani, kodi ndi zimene zimalowa m’kamwa kapena zimene zimatuluka m’kamwamo?
MUTU 57
Yesu Anachiritsa Mtsikana Komanso Munthu Wogontha
N’chifukwa chiyani mayiyu sanakhumudwe Yesu atayerekezera anthu a mtundu wake ngati tiagalu?
MUTU 58
Anachulukitsa Mikate Komanso Anachenjeza Ophunzira Ake za Zofufumitsa
Ophunzira a Yesu anamvetsa tanthauzo la zofufumitsa zimene Yesu ankawachenjeza nazo.
MUTU 59
Kodi Mwana wa Munthu Ndi Ndani?
Kodi makiyi a Ufumu n’chiyani? Ndani anawagwiritsa ntchito ndipo anawagwiritsa ntchito bwanji?
MUTU 60
Anaona Ulemelero wa Khristu Atasandulika
Kodi atumwi anaona chiyani m’masomphenya? Nanga zimenezi zinkatanthauza chiyani?
MUTU 61
Yesu Anachiritsa Mnyamata Amene Anali ndi Chiwanda
Yesu panafunika chikhulupiriro cholimba kuti mnyamata uja achiritsidwe n’chifukwa chake zinakanika poyamba paja. Koma kodi ndi ndani amene ankafunika kukhala ndi chikhulupirirocho, ndi mnyamatayo, bambo ake kapena ophunzira a Yesu?
MUTU 62
Kufunika Kokhala Wodzichepetsa
Anthu akuluakulu anaphunzira khalidwe lofunika kwambiri kwa kamwana kakang’ono.
MUTU 63
Yesu Anafotokoza Zoyenera Kuchita Anthu Akakhumudwitsana Komanso Ngati Wina Wachita Tchimo
Yesu anafotokoza malangizo amene abale ayenera kutsatira ngati wina wachita tchimo lalikulu.
MUTU 64
Anawaphunzitsa Kufunika Kokhululukira Ena
Yesu anagwiritsa ntchito fanizo la kapolo wopanda chifundo pofuna kusonyeza kuti Mulungu amatikhululukira ngati ifenso timayesetsa kukhululukira anzathu.
MUTU 65
Yesu Anaphunzitsa Anthu Ena Ali pa Ulendo Wopita ku Yerusalemu
Zimene Yesu anakambirana ndi anthu atatu omwe anakumana nawo m’njira, zingatithandize kudziwa zinthu zimene zingalepheretse munthu kuti akhale wotsatira wake.