Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo 1

Mawu Ofotokoza Chigawo 1

Baibulo limayamba n’kufotokoza zokhudza chilengedwe ndipo izi zimatithandiza kuyamikira zinthu zokongola zimene Yehova analenga zakumwamba komanso zapadzikoli. Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kuti athe kuzindikira mfundo yoti Mulungu analenga zinthu zodabwitsa zosiyanasiyana. Fotokozani kuti Mulungu anatilenga anthufe mwapamwamba kusiyana ndi zinyama. Anatilenga kuti tizitha kulankhula, kuganiza, kupanga zinthu, kuimba komanso kupemphera. Muthandizeninso kudziwa kuti Yehova ali ndi mphamvu, nzeru komanso chikondi. Ndipo amakonda zolengedwa zake kuphatikizapo ifeyo, aliyense payekha.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 1

Mulungu Analenga Kumwamba ndi Dziko Lapansi

Baibulo limati Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. Koma kodi ukudziwa kuti analenga mngelo uti asanalenge chilichonse?

MUTU 2

Mulungu Analenga Anthu Awiri Oyamba

Mulungu analenga anthu awiri oyamba n’kuiwaika m’munda wa Edeni. Ankafuna kuti iwo abereke ana ndipo kenako dziko lonse likhale paradaiso.